Malawi sisewera ndi Uganda
Chiyembekezo chidalipo kuti Malawi iswana ndi Uganda kuti ikonzekere masewero a World Cup pa 7 October pamene ikunthane ndi Tanzania.
Koma mlembi wa bungwe loyendetsa masewero m’dziko muno la FAM, Suzgo Nyirenda, walengeza kuti izi sizithekanso chifukwa osewera a Flames amene amasewera mpira wawo kunja kwa dziko lino sakwanitsa kudzasewera masewerowo chifukwa makalabu awo akhala otangwanika.
Malinga ndi Nyirenda, Flames idzanyamuka m’dziko muno ulendo ku Tanzania pa 4 October osachita zokonzekera ndi timu iliyonse.
Koma kochi wa timuyi, Ernest Mtawali, pofuna kupima mphamvu za anyamata ake, adakonza masewero ndi FISD Wizards Lachitatu ndipo Flames idapambana 4-0.
Flames idzakumananso ndi Tanzania pamasewero achibwereza pa 11 October pa Kamuzu Stadium mumzinda wa Blantyre.