Nation Online

Tuesday, May 21st

You are here: Home Tamvani

Nkhani

Maneb ikhutila ndi mayeso a sitandade 8

Bungwe loyendetsa mayeso la Malawi National Examinations Board (Maneb) lati lakhutira ndi mmene mayeso a Sitandade 8 ayambira.

Konvenshoni ya MCP yalephereka

Chipani cha Malawi Congress Party (MCP) chati msonkhano wake waukulu wa konvenshoni umene umayenera kukhalapo pakati pa lero ndi Lolemba wamwa madzi.

Anthu a ku Likoma alirira Ilala

Anthu okhala pazilumba za Likoma ndi Chizumulu ati akulira ndipo moyo ukutentha chifukwa cha kusiya kuyenda kwa sitima ya Ilala.

Zipolowe zikuphulika

Pamene tikuyandikira chaka cha 2014 pomwe Amalawi akuyembekeza chisankho cha magawo atatu chosankha Pulezidenti, aphungu a Kunyumba

Bajeti iganizire mavuto a anthu

Ndondomeko ya chuma ndiyo chiyembekezo chachikulu tsopano chomwe chingachepetse mavuto omwe anthu akukumana nawo kaamba ka kukwera mitengo ya zinthu m’dziko muno.

Wailesi ya Dzimwe ikusowa thandizo ku Mangochi

Nyumba youlutsira mawu ya Dzimwe Community Radio ku MonkeyBay m’boma la Mangochi yapempha thandizo lomangira ofesi komanso kugula zida zoulutsira mawu kuchokera kwa akufuna kwabwino.

‘Boma likweza malipiro’

Ogwira ntchito angasimbe lokoma ngati ganizo la unduna wa zantchito lokweza malipiro otsikitsitsa amene amalandira lingafitsidwe.

Konvenshoni ya MCP pa 28 April

Pamene chipani cha Malawi Congress Party (MCP) chatsimikiza kuti msonkhano wake waukulu wokasankha atsogoleri udzachitika pa 28 ndi 29 Epulo, katswiri wa zandale Dr Mustapha Hussein wadzudzula mchitidwe wosintha malamulo oyendetsera chipani n’cholinga chopatsa mpata anthu omwe sakuloledwa kupikisana nawo pamaudindo kuti atero.

Apolisi anjatidwa pokhudzidwa ndi ophedwa pa zionetsero

Apolisi asanu ndi anayi adatengedwa m’sabatayi powaganizira kuti akudziwapo kanthu pa za ena amene adaphedwa pazionetsero za pa 20 Julaye 2012.

Olephera asatuluke DPP—Mutharika

EMMANUEL MUWAMBAYemwe anali mtsogoleri wogwirizira mpando wa pulezidenti wa chipani cha DPP, Peter Mutharika, Lachinayi adalangiza omwe amapikisana nawo pofuna mipando yosiyanasiyana kuti akalephera si bwino kuchoka m’chipanicho.