Sunday, October 1, 2023
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

‘Mayi Mutharika ndi mlatho wa amayi’

by Albert Banda
28/06/2014
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Anthu osiyanayana ayamikira mtsogolerio wa dziko lino Peter Mutharika poganiza zokwatira atangopambana pachisankho cha pa 20 May ati chifukwa mayi wa fuko amathandiza mtsogoleri pogwira ntchito yotukula dziko.

Amayi ena omwe tidayankhulana nawo kumpingo wa St Michael’s and All Angels Lamulungu, komwe ukwati wa awiriwua udamangidwa mumzinda wa Blantyre, adati kubwera kwa Mayi Gertrude Mutharika kwatsegula khomo lina loti amayi aziperekerako madadandaulo awo komanso kupempha zinthu zina zachitukuko.

Mayi Mutharika
Mayi Mutharika

Phungu wogonja pampando wa uphungu kudera la kumadzulo kwa mzinda wa Blantyre, Bertha Masiku, adati ali ndi chikhulupiriro kuti Mayi Mutharika athandiza dziko lino makamaka polimbikitsa ntchito za amayi ndipo adalangiza anzawo onse ogonja kuti aganizire zothandiza boma posayang’anira chipani chawo.

“Tiyamikire a Pulezidenti komanso mayi a kunyumba kwawo pogwirizana kuti athandizane potukula dziko. Pachikhalidwe chathu, timadziwa kuti pempho lodzera mwa amayi limadutsa kwa abambo. Amayi tili ndi chiyembekezo kuti mtsogoleri wa dziko lino apereka chilichonse kudzera mwa mayi wa fukoyu pothandiza ntchito zotukula miyoyo ya amayi,” adatero Masiku.

Woyang’amira ntchito za uchembere wabwino m’dziko muno, Dorothy Ngoma, naye adayamikira mtsogoleri wa dziko lino ndipo adati izi zithandiza pantchito za amayi. Iye adati popanda mayi kunyumba yachifumu chidwi pankhani za umoyo wa amayi zidakakhala zochepa popeza ntchito zambiri zachitukuko m’dziko muno zimadalira chidwi kuchokera kwa atsogoleri.

“Pokhala mayi wa fuko, tili ndi chikhulupiriro kuti azitiyankhulira pankhani zosiyanasiyana zokhudza amayi, makamakanso pomwe dziko likutaya miyoyo yambiri chifikwa cha kusowa kwa zipangizo zothandizira amayi oyembekezera ndi zina,” adatero Ngoma.

Iye adati dziko lino likutaya amayi pakati pa 3 000 ndi 4 000 pazifukwa za uchembere komanso matenda ena monga HIV ndi Edzi, khansa ndi TB.

Phungu wogonja ku Mulanje Pasani Peter Nowa adati nzonyaditsa kuti mayi wa fuko ndi mayi woti adakhalapo m’Nyumba ya Malamulo ndipo akudziwa mavuto amene aphungu ngakhalenso makhansala amakumana nawo akamapempha zinthu zina.

Iye adati mbiri ya mayiyu ikuonetsa kuti ndi wolimbikira ndipo pali chiyembekezo chachikulu kuti athamangathamanga ndi kugwira ntchito ndi athu onse pokweza dziko lino.

Previous Post

MCP yakhumudwa ndi kasankhidwe ka nduna

Next Post

Esther Mcheka-Chilenje, first deputy speaker of parliament

Related Posts

Nkhani

 Ma rodibuloku abwerere

September 29, 2023
To be buried on Wednesday: Tembo
Nkhani

A Tembo asiya Amalawi m’misozi

September 29, 2023
Nkhani

 Liwu la mafumu pa zochotsa anthu 1 miliyoni mu AIP

September 23, 2023
Next Post
Tipped for Speaker
position: Chilenje

Esther Mcheka-Chilenje, first deputy speaker of parliament

Opinions and Columns

My Turn

Unpacking street language

September 29, 2023
My Turn

Unpacking street language

September 29, 2023
Columns

‘Cancel the debts…cancel the debts’

September 27, 2023
My Turn

Making tourism sector tick

September 27, 2023

Trending Stories

  • Banda: We are on watch list
following misreporting

    Troubled kwacha sheds off 4.7%

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • President to lead in mourning Tembo, burial Wed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  •  Govt ponders maize imports

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  •  Chakwera sits on peace commission

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi unveils inaugural electric vehicle, Citroen e-C3

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2023 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.