Friday, August 19, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Alimi samalani thonje, kwagwa kachilombo koononga

by Bobby Kabango
09/05/2015
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Kwatulukira kachilombo kotchedwa kodikodi kapena kuti mealybug kamene kakuononga thonje, watero mlembi wamkulu wa unduna wa malimidwe Erica Maganga.
Maganga wati kachilomboka kakuumitsa mitengo ya thonje komanso nkhunje za thonje zikumaphulika zisanakhwime zomwe zikuchepetsa zokolola.
Madera ambiri kunsi kwa mtsinje wa Shire monga ku Magoti EPA m’boma la Nsanje komanso ku Lisungwi EPA m’boma la Neno ndi komwe tizilomboni tagwa ndipo thonje lambiri lauma.
Malinga ndi Maganga, thonje la mtundu wa Chureza lomwe lili ndi maluwa komanso lopanda maluwa ndi lomwe lagwidwa kwambiri ndi tizilomboti.
Maganga wati tizilomboti tikumabisala m’ming’alu komanso m’mauna kapena mopindika mwa mbewu zomwe zikuchititsa kuti alimi alephere kutiona.

Mlimi kusamalira thonje lake
Mlimi kusamalira thonje lake

Mlembiyu akuti kupha kwa tizilomboti ndi kovuta chifukwa cha momwe tidabadwira.
“Timakhala ndi mafuta pa khungu lake komanso taufaufa zomwe zimateteza tizilomboti ku mankhwala ndi ku nyengo ina iliyonse yobweretsa chiopsezo ku tizilomboti,” adatero Maganga.
Malinga ndi mlembiyu, sizikudziwika kuti kachiromboka kachecheta ndime yaikulu bwanji chifukwa undunawu ukadafufuza chionongekocho.
Komabe Maganga wati alimi apopere minda yawo mankhwala a Acephate, 75 SP 1gm/L kapena Malathion 50 EC 2ml/L pa mlingo wa mamilimita 250 pa hekitala kapena maekala awiri ndi theka pogwiritsa ntchito mlingo wa 17.5l wa mankwhalawa mumalita 14 a madzi.
Iye wati tizilomboti timafala kudzera mumbewu ya thonje, mphepo, madzi omwe amagwiritsira ntchito, madzi a mvula, mbalame, anthu komanso ziweto.
M’kalata yomwe undunawu watulutsa, tizilomboti timapezeka m’mitengo ya maluwa, zipatso, mbewu zakudimba ndi kumunda komanso m’tchire.
“Tikulangiza alimi kuti aonetsetse kuti m’minda ndi mosamalika. Alambule tchire lonse lozungulira munda wa thonje, azule ndi kuotcha mitengo ya thonje akangomaliza kutola thonje. Azule ndi kuotcha mitengo yonse ya thonje yogonera m’munda, abzale thonje mwakasinthasintha, agwiritse ntchito mbewu ya thonje yovomerezeka, komanso abzale chimanga kapena nandolo mozungulira munda wa thonje,” adatero Maganga pamene wapempha alimiwa kuti azifunsa alangizi a m’dera lawo ngati zasokonekera.

Tags: achukumbeThonjeUlimi
Previous Post

What or who?

Next Post

Muli phindu mu ulimi wa chinangwa

Related Posts

Patrick sakubwerera mmbuyo pa chikopa
Nkhani

Patrick Mwaungulu ndi katakwe pokankha chikopa

July 24, 2022
Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Next Post

Muli phindu mu ulimi wa chinangwa

Opinions and Columns

My Turn

Diagnostic tech cost on patients

August 19, 2022
Business Unpacked

Why public debt should worry every patriotic Malawian

August 18, 2022
Rise and Shine

How to triumph in interviews

August 18, 2022
My Turn

Making briquettes at Malasha

August 15, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Court snubs tenants on govt houses

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • ‘Blantyre derby could have fetched more’

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Why graft cases stall

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • World Bank protests K14bn ICT contract

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Govt appoints university working committee

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.