Tuesday, August 9, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Anatchezera

by ANATCHEZERA
27/09/2015
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Sakundikwatira

Agogo,

Ndithandizeni. Ndili paubwenzi ndi mwamuna yemwe adakwatirapo koma banja lake lidatha ndi mkaziyo ndipo kuli mwana mmodzi. Inenso ndili ndi mwana mmodzi. Titatha chaka tili pachibwenzi adandiuza kuti andikwatira koma mpaka lero padutsa zaka 4 palibe chimene chkuchitika. Foninso adasiya kundiimbira, komanso pan chikondi chachepa. Nditani?

BH

 

Zikomo BH,

Mwamunayo si wachilungamo ndipo akungokunamiza, za banja alibe nazo ntchito. Ngati ukuti pano zaka 4 zatha chikuuzireni kuti akufuna akukwatire ndipo olo foni sakukuimbiranso, ufuniranji umboni wina woti alibe nawe chikondi? Usataye naye nthawi ameneyo, udzangodikirapo madzi a mphutsi apa. Palibe chako. Akadakhala kuti ali ndi chidwi nawe pano atakaonekera kwa makolo ako ndipo pano bwenzi tikukamba kuti muli pabanja.

 

Ndidalirebe?

Agogo,

Ndifunse nawo. Ine kwathu ndi ku Rumphi ndipo ndakhala ndili pachibwenzi ndi mnyamata wa ku Mzimba kwa zaka ziwiri tsopano. Sitinagonanepo ndipo tinagwirizana zotengana koma mpaka pano chaka chikuthanso. Ndikamufunsa akuti akonzeke kaye. Kodi ndipange bwanji? Ndidalirebe?

 

Zikomo pondilembera kuchoka ku Rumphiko. Funso lovuta kuyankha mwana wanga—kodi udalirebe? Inde ndikuti eee, usataye mtima poti kuona maso a nkhono n’kudekha. Ngati mnyamatayo akuti akonzeke kaye, mwina akunena chilungamo. Ndi anyamata ochepa amene amatha kukhala pachibwenzi ndi mtsikana kwa zaka ziwiri osagonana naye. Sindidziwa, paja amati mtima wa mnzako ndi tsidya lina, koma mmene ndikuonera fatsa, zoona zake zioneka zokha. Iwe ukuthamangira banja chifukwa chiyani? Mwamunayo ngwanzeru n’chifukwa chake akuti akonzekere kaye za ukwati, osangoti lero ndi lero basi tikwatirane uku alibe chilichonse. Ndikudziwa bwino lomwe kuti ku Mzimba ndi ku Rumphi miyambo yokhudza ukwati imafanana, mwamuna akafuna kukwatira amayenera kupereka malobolo, si choncho? Ndiye mwina akusakasaka kaye kuti akamatuma ‘thenga’ kwa asewere akhale ndi kenakake m’manja, osati kungopita chimanjamanja. Chachikulu n’choti simudagonanepo ndipo ngati ukuona kuti akukunamiza ukhoza kumusiya n’kupeza wina amene watsimikiza za ukwati. Nthawi zambiri atsikana ena zikawavuta, tiyese kuti mwatsoka achimwitsidwa ndi wina pamene ali pachibwenzi ndi winanso, amakakamira wachikondiyo kuti akwatirane msangamsanga n’cholinga choti azikati pathupi mpamwamunayo! Ndikhulupirira sizili chonchi ndi iwe.

 

Ofuna Mabanja

 

Ndine mayi wa mwana mmodzi ndipo ndikufuna mwamuna wodziwa mavuto, wachikondi, woopa Mulungu koma wopanda banja. – 0884 437 604

 

Ndili ndi zaka 23 ndipo ndifuna mwamuna woti ndimange naye banja. Akhale woti akufunadi banja osati zoyesana ayi. Wofuna aimbe pa:

0992 673 004

 

Ndine mayi wa ana awiri ndipo ndifuna mwamuna womanga naye banja. Akhale wachilungamo komanso woopa Mulungu.0992 728 276

Previous Post

Rosier than Orwell’s Animal Farm

Next Post

Gayighaye Mfune: Wosula oimba

Related Posts

Patrick sakubwerera mmbuyo pa chikopa
Nkhani

Patrick Mwaungulu ndi katakwe pokankha chikopa

July 24, 2022
Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Next Post
Mfune: Ndimafuna kuti oimba apite patali

Gayighaye Mfune: Wosula oimba

Opinions and Columns

My Turn

Bitcoin and regulations

August 8, 2022
Editor's Note

My beautiful experience as an intern

August 7, 2022
Editor's Note

My beautiful experience as an intern

August 7, 2022
Big Man Wamkulu

What is he up to? He doesn’t drink

August 7, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Macra ordered MultiChoice Malawi not to 
implement the new proposed tariffs

    Court rebuffs MultiChoice Malawi on new tariffs

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Treasury Secretary says won’t resign

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Judiciary under probe 

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chakwera’s austerity measures questioned

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Nankhumwa rally irks DPP governor

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.