Thursday, August 11, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Fodya wakunja wayamba kulowa

by Martha Sande
02/06/2017
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Pomwe dziko la Malawi lalima fodya wochepa ndi makilogalamu 27 miliyoni pamlingo omwe ogula fodyayu adaitanitsa, mavenda ena amachawi ayamba kulowetsa fodya kuchoka m’maiko oyandikana ndi dziko lino.

Fodyayu akumalowetsedwa pogwiritsa ntchito njira zozemba chifukwa mchitidwewu  ngosemphana ndi malamulo a dziko lino.

Wogwirizira udindo wa mkulu wa bungwe loyendetsa ulimi wa fodya m’dziko muno la Tobacco Control Commission (TCC) David Luka adati bungwe lake likudziwa za mchitidwewu ndipo lidatumiza maofesala ake kumalo onse omwe izi zikuchitika.

“Maofesala athu ali ku Nkhamenya, m’boma la Kasungu komwe kumalowera fodya kuchokera m’dziko la Zambia ndipo ena ali ku Mchinji komanso ku Namwera m’boma la Mangochi komwe fodya wake amakhala ochokera ku Mozambique,” adatero Luka.

Iye adati bungwe lake ndi lokhumudwa ndi mchitidwewu omwe uli vuto lalikulu pa ulimi wa fodya m’dziko muno.

“Ntchito  yoyesetsa kuti fodya asalowe kapena kutuluka m’dziko muno siyapafupi, ndipo sikwapafupi kuchitapo kanthu” adatero Luka.

Iye adaonjezeranso kuti nkhanizi kwambiri ndi zokhudza dziko ndi dziko linzake.

Alimi a fodya ena m’boma la Mchinji adatsimikiza za kulowa kwa Fodya m’dziko muno.

Mmodzi mwa alimiwa, Lazarus Chitedze, yemwe wakhala akulima fodya kwa zaka pafupifupi 20 adati fodyayu akulowa pang’ono chabe kuchokera m’dziko la Zambia kusiyana ndi momwe zimakhalira zaka zonse.

“Akulowetsa fodya ndi mavenda ang’onoang’ono omwe amagwiritsa ntchito njinga, mwina chifukwa chakuti m’maliremu muli asilikali omwe akulondera chimanga kuti chisatuluke,” adatero Chitedze.

Iye adati chaka ndi chaka fodya amalowa kuchokera ku Zambiako kapena kutuluka kuchoka m’dziko muno.

“Zimatengera komwe msika uli bwino chaka chimenecho.Ngati ku Zambia zili bwino, mavenda amazembetsa fodya kupita naye komweko,” adatero Chitedze.

Iye adati zikatere zimawakomera alimiwa chifukwa mavendawa amawagula mokwera mtengo kusiyana ndi ku msika wa fodya.

Malinga ndi Chitedze, chiopsezo chimakhalapo fodya akamalowa kuchokera m’dzikolo chifukwa zikhonza kuchulutsa fodya pamsika kuposera mlingo omwe ogula akufuna.

Polankhulapo mlimi wina yemwe sadafune kutchulidwa dzina lake adati fodyayu akulowa pang’ono chifukwa ku Zambiako ayamba kumene kusankha fodya.

“Akangoti wafika pachimake kumeneko, timuona akulowa wochuluka zedi,” adatero mlimiyo.

Mwezi wathawu, woyan’ganira dera la kummawa m’boma la Zambia Chanda Kasolo adauza ena mwa atolankhani a dzikolo kuti asilikali omwe ali m’malire a dziko lino ndi dzikolo akutetezanso kuzembetsa fodya.

Dziko la Zambia lidalengeza chaka chathachi kuti likweza mlingo wa fodya yemwe amalima kuchoka pa ma kilogalamu 23 miliyoni kufika pa 30 miliyoni chaka chino.

Ndipo chaka chathachi mtsogoleri wa bungwe la alimi la Eastern Fodya Association of Zambia (Efaz) Franklyn Mwale adadandaulira bungwe loyendetsa ulimi wa fodya m’dzikolo kuti msika wawo amautsekula mochedwa poyerekeza ndi wa dziko lino.

Koma limodzi mwa mabungwe a alimi la Tobacco Association of Malawi (Tama) lidati silidalandire lipoti lililonse lokhudza kulowa kwa fodya kuchokera mdziko la Zambia.

Previous Post

Malawi ranks lowly on childhood index

Next Post

‘Ndalama zaperewera m’magawo ofunikira’

Related Posts

Patrick sakubwerera mmbuyo pa chikopa
Nkhani

Patrick Mwaungulu ndi katakwe pokankha chikopa

July 24, 2022
Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Next Post
Ana ena akuphunzira m’zisakasa ngati izi

‘Ndalama zaperewera m’magawo ofunikira’

Opinions and Columns

Business Unpacked

How government is killing parastatals softly

August 11, 2022
Rise and Shine

Victor Cheng on mental energy units

August 11, 2022
My Turn

Bitcoin and regulations

August 8, 2022
Editor's Note

My beautiful experience as an intern

August 7, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Chizuma: She had medical consultations

    ACB clarifies Buluma’s absence for trial

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Agriculture lessons from advanced countries

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Registrar corners political parties

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Biz Fantasy Premier League returns

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Withdraw motion on Judiciary—CSOs

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.