Monday, December 4, 2023
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
  • Mother’s Fun Run
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
  • Mother’s Fun Run
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Kupewa chigodola cha nkhumba ndikotheka

by ESMIE KOMWA
11/05/2019
in Chichewa
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

M’mwezi wa February chaka chino mlimi wina wa nkhumba m’boma la Lilongwe, Jeofrey Kaiyatsa, adaona ngati malodza nkhumba zake zonse zitafa ndi chigodola.

Panthawiyo n’kuti ali ndi nkhumba zazikulu zosachepera 30. Funso n’kumati: kodi zidamuvuta pati?

“Ndikuganiza kuti mnyamata yemwe ndidamulemba ntchito yosamalira nkhumbazi samayenda bwino choncho adakatenga matendawa kwina n’kulowetsa m’makola.

Tetezani nkhumba zanu ku chigodola

“Ku Lilongwe kuno sindikhalitsako chifukwa ndimachitanso ulimi wa mtundu womwewu ku Blantyre kotero kumakhala kovuta kumuyang’anira mnyamatayu,” adadandaula motero mlimiyu.

Padakali pano mlimiyu ali ku Lilongwe ndipo akukonza makola n’cholinga choti ayambirenso kuweta pogwiritsa ntchito mbewu yomwe ali nayo ku Blantyre.

Ngakhale  chigodola cha nkhumba chilibe mankhwala, mphunzitsi wa za ulimi wa ziweto wa ku Lilongwe University of Agriculture and Natural Resources (Luanar), Jonathan Tanganyika, akuti matendawa ndi opeweka.

Malingana ndi Tanganyika, mlimi asunge ndi kudyetsera nkhumba zake m’khola, asalole munthu wina aliyense kupita ku khola lake, asabweretse nyama ya nkhumba ku makola, komanso asagule nkhumba kapena chakudya chake m’mudzi momwe mwagwa chigodola.

“Kuonjezera apo, mlimi sayenera kupita kukhola la mlimi mnzake kuopetsa kutengako matendawa,” iye adatero.

Tanganyika adafotokozanso kuti ngakhale mlimi atatsimikizika kuti kumalo komwe wagula nkhumba za mbewu kulibe chigodola, akuyenera kuzisunga padera kwa masabata awiri ndipo akaona kuti sizikuonetsa chizindikiro chilichonse cha matendawa akhoza kuzisakaniza ndi zakale.

Woona za ulimi wa ziweto ku Machinga Agricultural Development Division (Maadd) Edwin Nkhulungo adafotokoza kuti mlimi yemwe nkhumba zake zidatha ndi chigodola ndipo akufuna kuyambiranso amayenera akhale osamala chifukwa kupanda kutero, vutoli lizingopitirirabe.

Iye adati mlimi ayenera kukonza bwino makola asadaikemo nkhumba zina kuopetsa nkhupakupa zomwe zimafalitsanso matendawa.

“Mlimi achotse ndowe zonse ndipo ngati n’kotheka asuke zodyera ndi zomwera nkhumba,” Nkhulungo adatero.

Mkuluyu adafotokoza kuti ngati mlimi ali ndikuthekera akhoza kutentha makola akalewo ndikukamanga ena atsopano kutali kuti asakhale pachiopsezo cha matendawa.

Tanganyika adaonjeza kuti m’khola mukalowa chigodola, mlimi ayenera kupha nkhumba zonse zodwala ndikukwirira msanga.

Iye adati malo wopherawo akuyenera kukhala wobisika, komanso wotchingidwa bwino kuti nkhumba zisafikepo.

“Tizilombo toyambitsa matendawa timakhalirira pamalo pomwe paphedwa nkhumbazo ndipo ngakhale patapita masabata angapo, nkhumba zamoyo zikafika zimatenga tizilomboti n’kuyamba kudwala,” iye adatero.

Mphunzitsiyu adafotokoza kuti nkhumba zamoyo  za m’khola limodzi ndi zodwalazo zikuyenera kuphedwa ndipo nyama yake anthu akhoza kudya kapena kugulitsa.

Malingana ndi Tanganyika, chigodola n’choopsa kwambiri chifukwa chimapha nkhumba zambiri m’kanthawi kochepa.

Mlili wa matendawa umagwa m’chaka chilichonse choncho umaopseza ulimi wa nkhumba.

Matendawa amafala kuzera mu nyama, mafupa ndi ubweya ya nkhumba yodwala ndipo chilichonse chokhudzidwa ndi zinthuzi chimanka nichifalitsa matendawa.

Kuonjezera apo, nkhupakupa zopezeka m’khola la nkhumba ndi nguluwe zimafalitsa matendawa.

Iye adaonjeza kuti zina mwa zizindikiro za matendawa ndikunyentchera, kufooka, kupeperuka poyenda,komanso kulengeza magazi pa khungu.

Tanganyika adati nkhumba zimafa zikangodwala kanthawi kochepa ndipo zina zimangofa mwadzidzidzi osaonetsa zizindikiro.

Potsiriza, katswiriyu adati mlimi ayenera kuthamangira kwa alangizi a ziweto a m’dera lake akaona zoterezi.

Previous Post

Five worst roads: why are they missing on the political campaign agendas?

Next Post

Economists caution on Treasury Bills rise

Related Posts

Nkhani

 Amanga 10 pa mkangano wa ufumu

December 2, 2023
Nkhani

Mitala iphetsa

November 25, 2023
Made the contribution in his personal capacity: Chakwera
Nkhani

 Chiyembekezo chakwera ndi mawu a Chakwera

November 18, 2023
Next Post
Kalilombe: It may cost more

Economists caution on Treasury Bills rise

Opinions and Columns

People’s Tribunal

We haven’t learnt lesson on holding protests

December 3, 2023
Musings on Corruption

Beware of social norms, pluralistic ignorance

December 3, 2023
Big Man Wamkulu

He named our kid after girlfriend

December 3, 2023
Guest Spot

‘MPs must scrutinise IMF deals’

December 2, 2023

Trending Stories

  • OPC under scrutiny over recruitment

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chakwera mulls over Zamba chop calls

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • AfDB to support Malawi’s economic infrastructure

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chaos at ‘Is the President Dead’ movie premiere

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • He named our kid after girlfriend

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
Loading
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2023 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
  • Mother’s Fun Run

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.