Sunday, October 1, 2023
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Mabungwe apereke nzeru pamkangano wa nyanja

by Johnny Kasalika
06/10/2012
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Kadaulo wa mbiri yakale, Kings Phiri, wati ndibwino dziko lino lipemphe bungwe la umodzi wa maiko a mu Africa la African Union (AU) kuti likhale mkhalapakati pa zokambirana za umwini wa nyanja ya Malawi yomwe dziko la Tanzania likuti likufunapo gawo.

Phiri walankhula izi mtsogoleri wa dziko lino, Joyce Banda atanena kuti palibenso zokambirana pa umwini wa nyanjayi kotero nkhaniyi ikuyenera kukakambidwa ku bwalo lalikulu la milandu padziko lapansi.

Pouza atolankhani Lachiwiri pomwe amachokera ku United States, Banda adati waona kuti zokambirana pakati pa maikowa sikuphula kanthu kotero ndibwino bwalo lamilandu likaweruze lokha.

“Pamene ndimachoka m’dziko muno ndidali ndi lingaliro kuti nkhaniyi yatha koma osadziwa kuti yakula,” adatero Banda, akumveka wodabwa ndi nkhaniyi.

Koma Phiri wati m’malo modya mfulumira ndi bwino kupempha mabungwe monga la AU kapena SADC kuti akhale pakati pa zokambiranazo.

“Sindikutanthauza kuti ganizo la mtsogoleriyu ndilolakwika, koma titayamba tayesa izi mwina zingatithandize,” adatero Phiri.

Nyakwawa Mwanayaya ya kwa T/A Makhwira m’boma la Chikhwawa yati ikugwirizana ndi maganizo a Banda kuti nkhaniyi ipite kubwalo lamilandu chifukwa kumeneko ndiko kukathe zonse.

“Tichedwa nazo kuti tifufuzenso kwina, ndibwino bwalo likaweruze basi,” adatero Mwanayaya.

Mkangano wa dziko la Malawi ndi Tanzania udayamba pomwe dziko lino lidayamba kufufuza mafuta panyanja ya Malawi.

Apa dziko la Tanzania lidaletsa ntchitoyo ponena kuti nyanjayi ndiyogawana.

Zokambirana pofuna kupeza mutu wa nkhani zidayambika m’dziko muno pomwe mamulumuzana a dziko la Tanzania adafika m’dziko muno.

Chikonzero chidali choti zokambiranazi zikachitikenso m’dziko la Tanzania pomwe akuluakulu a dziko lino amayembekezera kupita kumeneko.

Previous Post

Delays mar Blantyre Arts Festival launch

Next Post

Femia Kazembe (Anaziya)

Related Posts

Nkhani

 Ma rodibuloku abwerere

September 29, 2023
To be buried on Wednesday: Tembo
Nkhani

A Tembo asiya Amalawi m’misozi

September 29, 2023
Nkhani

 Liwu la mafumu pa zochotsa anthu 1 miliyoni mu AIP

September 23, 2023
Next Post
The Nation Online Femia Kazembe (Anaziya)

Femia Kazembe (Anaziya)

Opinions and Columns

My Turn

Unpacking street language

September 29, 2023
My Turn

Unpacking street language

September 29, 2023
Columns

‘Cancel the debts…cancel the debts’

September 27, 2023
My Turn

Making tourism sector tick

September 27, 2023

Trending Stories

  • Banda: We are on watch list
following misreporting

    Troubled kwacha sheds off 4.7%

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • President to lead in mourning Tembo, burial Wed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  •  Govt ponders maize imports

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  •  Chakwera sits on peace commission

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi unveils inaugural electric vehicle, Citroen e-C3

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2023 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.