Friday, August 12, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Malawi ali pamoto—Kapito

by Staff Writer
07/01/2012
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Mkulu wa bungwe loona ufulu wa ogula la Consumers Association of Malawi (Cama), John Kapito wati boma likuyenera kutulutsa chimanga chomwe chikusungidwa m’khokwe zake kuti anthu ayambe kugula chimangachi pa mtengo wotchipa ku Admarc.

Kapito walankhula izi m’sabatayi potsatira ganizo la bungwe la Admarc lokweza mtengo wa chimangachi.

Pa 21 Disembala, bungweli lidakweza mtengo wa chimanga.

Thumba lolemera makilogalamu 50 lidayamba kugulitsidwa pa K3 000 kuchoka pa K2 000.

Apa Kapito waunikira kuti uku ndikupha kapena kulanga Amalawi pomwe asadalakawe.

Iye wati chimanga chomwe bungwe la Admarc likukweza ndichomwe lidagula lokha kutsatira kulephera kwa boma kupereka ndalama ku bungweli.

“Nkhaniyi ndiyovutirapo chifukwa choti chimanga chidasamutsidwa kuchoka ku Admarc kupita ku boma.

“Chimanga chomwe chimasungidwa ndi Admarc sichaboma. Chimanga cha boma chimakhala kunkhokwe zaboma, ndiye aboma ndiwo amauza a Admarc kuti awagulitsire.

“Chimangachi Admarc idagula yokha ndi ndalama zawo kuchokera ku banki chifukwa choti boma lidakana kuwapatsa ndalama.

“Tisayang’ane Admarc, koma tiyang’ane boma kuti litulutse chimanga chimene chilipo munkhokwe; pajatu boma limati amanga nkhokwe momwe muli chimanga chambiri,” adatero Kapito.

Iye adati izi zikachitika, kumsika wa Admarc kukhala chimanga chotsika mtengo.

Kapito wati vuto lina n’kuti boma lidagulitsa chimanga kunja, zomwe zachititsa kuti chimanga chiyambe kusowa m’dziko muno.

Mavenda nawo akwezanso mitengo.

Ku Mbayani mumzinda wa Blantyre, thumba la chimangali lili pa K3 500 kutsatira kukweza kwa a Admarc.

Lawrence Mizati wa m’mudzi mwa Chimbeta kwa T/A Changata m’boma la Thyolo wati kukweraku kukhudza anthu ambiri chifukwa kwadza nthawi yomwe mavuto m’dziko muno ali posasimbika.

Caroline Malemia wa m’mudzi mwa Mdala kwa T/A Machinjiri m’boma la Blantyre wati kudera lawo chimangachi chakwera kwambiri, maka mwa mavenda, zomwe zikuika moyo wawo pachiopsezo.

“Kilogalamu ya chimanga ili pa K80 kuchoka pa K55; thumba lili pa K4 000. N’kovuta kuti omwe ali ndi mabanja akulu akwanitse kugula.

“Zinthu sizili bwino kotero boma likuyenera kuganizira omwe tikuvutika,” adatero Malemia.

Previous Post

Netball leagues await new rules

Next Post

Association to revamp car hire industry

Related Posts

Patrick sakubwerera mmbuyo pa chikopa
Nkhani

Patrick Mwaungulu ndi katakwe pokankha chikopa

July 24, 2022
Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Next Post
The Nation Online Association to revamp car hire industry

Association to revamp car hire industry

Opinions and Columns

Bottom Up

Mindset change should target Indian-Malawians

August 12, 2022
My Turn

Legalise cannabis for poor farmers

August 12, 2022
Editor's Note

Govt set to develop Whistleblower Protection Act

August 11, 2022
Business Unpacked

How government is killing parastatals softly

August 11, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Chakwera withheld delegated duties from Chilima

    Did ACB, LMC rush? 

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • K1bn organic fertiliser plant rolls into action

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Anti-judge vibe worries judiciary

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Minister allays Shoprite exit fears

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • How government is killing parastatals softly

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.