Monday, September 25, 2023
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Pemphererani dziko lino, ipempha ECM

by Staff Writer
25/02/2012
in Nkhani
1 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Mpingo wa katolika wapempha Amalawi kuti apempherere dziko la Malawi ndi utsogoleri wadziko lino panyengo ya Lenti.

Muuthenga wake wanyengoyi, mkulu wa mabishopu m’gulu la Episcopal Conference of Malawi (ECM) Joseph Zuza wati padakali pano, Amalawi akudutsa mumazunzo.

Zuza adati: “Atsogoleri athu ali ndi udindo waukulu woti moyo uzikhala ofewa wa ife tonse. Monga okhulupirira tiyenera kudziwa kuti Mulungu sangatitaye.”

Zuza adati zina mwa zomwe Amalawi ayenera kupempherera kuti zichepe ndi katangale ndi ziphuphu, kukondera ochokera kudera kwanu, kusankhana mitundu, zilakolako zakuthupi, ufiti, nkhanza kwa ana, uchidakwa ndi kupembedza Satana.

Zuza adapempha akatolika kuti aziyesetsa kukhala Akhristu achitsanzo, ndikutsatira malamulo a Mulungu.

“Aliyense ayenera kuonetsetsa kuti akukhala okhulupirika pamaso pa Mulungu,” adatero Zuza.

Ndipo muuthenga wake m’nyengoyi, Papa Benedict wachikhumi ndi chisanu n’chimodzi adati masiku 40 amene Akatolika akhale akupunguza ayenera kulingalira za mawu opezeka pa Ahebri 10 ndime 24.

“Tiyenera kukhudzidwa ndi mavuto a ena; kukhala okondana kumanso kugwira ntchito zabwino,” adatero Papayo.

Kwa masiku 40, Akatolika amakhala akupunguza ndipo zimayamba ndi tsiku la phulusa, lomwe lidali Lachitatu.

Panthawiyo, iwo amakhala akupemphera, kugawana, kulingalira molimba, kusala komanso kuchita zachifundo mpaka nthawi ya Pasaka mu Epulo.

Previous Post

Group One to create 1 000 new jobs

Next Post

‘I know what people want’

Related Posts

Nkhani

 Liwu la mafumu pa zochotsa anthu 1 miliyoni mu AIP

September 23, 2023
Nkhani

Boma likugwiritsa K3 biliyoni pothandiza ochotsa mimba

September 23, 2023
Gogo Chabwera
Nkhani

Gogo athawa m’mudzi mwake

September 17, 2023
Next Post

‘I know what people want’

Opinions and Columns

My Turn

Resolve DStv spat amicably

September 25, 2023
People’s Tribunal

Time for politicians to memorise the myth of Sisyphus

September 24, 2023
Big Man Wamkulu

I hear he is engaged to somebody

September 24, 2023
Musings on Corruption

Is ‘God-fearing’just a façade?

September 24, 2023

Trending Stories

  • I hear he is engaged to somebody

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Just kill me—cries Cashgate convict

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Govt sluggish on multi billion loss-cutting law

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Mysterious animal injures 9 people

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • DPP, ACB working to revoke Mphwiyo’s bail

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2023 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.