Thursday, August 11, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Zizindikiro za kufa kwa ziwalo

by ESMIE KOMWA
05/01/2019
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Dotolo wa pa chipatala cha Gulupu m’boma la Blantyre, Lerato Mambulu, wati kufa kwa ziwalo nthawi zambiri kumachitika mwadzidzidzi.

Pachifukwa ichi, kumakhala kovuta munthu kumva kapena kuonetsa zizindikiro zoti afa ziwalo.

“Munthu amatha kungomva kupweteka mutu ngati amumenya mwina ndi chitsulo ndikugwa pansi basi kufa kwa ziwalo n’kukhala komweko,” iye adatero.

Mambulu adafotokoza kuti izi zimachitika kwa anthu amene misempha yawo ya magazi yaphulika mbali ya thupi yomwe yafayo.

Iye adati misemphayi ikaphulika, magazi sayenda kupita ku ubongo zotsatira zake sipakhala kulumikizana kulikonse pakati pa ubongo ndi mbali yomwe sikukufika magaziko.

Dotoloyu adati zinthu zikafika pamenepa mbaliyo imaleka kugwira ntchito.

“Anthu ena amatha kufa ziwalo kapena kusiya kuyankhula kwa maola ochepa okha ndikuchira. Ichi ndi chizindikiro chachikulu cha matendawa,” iye adatero.

Mambulu adati izi zili chomwechi chifukwa anthu oterewa amakhala pachiopsezo chachikulu choti atha kuzakhala ndi vutoli mokhazikika mtsogolo.

Pachifukwa ichi, dotoloyu adati munthu akaona izi, asazitenge mwa chizolowezi kuti ndi momwe ndimachitira, koma athamangire ku chipatala kukapeza thandizo kuti mtsogolo, lisadzakhale vuto lokhazikiza.

Iye adati ngakhale izi zili chomwechi, ndi anthu ochepa okha omwe amatha kuyamba motere.

“Kwa anthu omwe BP yawo imakhala yokwera ndipo amamva kuwawa kwa mutu kwambiri, nkhope imatha kuonetsa zizindikiro zofooka kusonyeza kuti nthawi ina iliyonse, ziwalo zikhoza kufa,” iye adatero. Tsabata ya mawa tizafotokoza zinthu zomwe zimamuika munthu pa chiopsezo cha matenda a kufa kwa ziwalo. 

Previous Post

UN condemns albino killings

Next Post

Public institutions that made Malawians smile in 2018

Related Posts

Patrick sakubwerera mmbuyo pa chikopa
Nkhani

Patrick Mwaungulu ndi katakwe pokankha chikopa

July 24, 2022
Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Next Post

Public institutions that made Malawians smile in 2018

Opinions and Columns

Business Unpacked

How government is killing parastatals softly

August 11, 2022
Rise and Shine

Victor Cheng on mental energy units

August 11, 2022
My Turn

Bitcoin and regulations

August 8, 2022
Editor's Note

My beautiful experience as an intern

August 7, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Chizuma: She had medical consultations

    ACB clarifies Buluma’s absence for trial

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Agriculture lessons from advanced countries

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Registrar corners political parties

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Biz Fantasy Premier League returns

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Withdraw motion on Judiciary—CSOs

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.