Wednesday, October 4, 2023
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Kupherera ng’amba ndi Akalozera m’munda

by Temwa Mhone - Correspondent
01/09/2018
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

 

Alangizi a zaulimi apempha alimi m’dziko muno kuti azipanga akalozera kuti ateteze nthaka, komanso kusunga chinyontho kwa nthawi yaitali m’minda yawo.

Madalitso Munthali, mlangizi wa mbewu ku Kaporo m’boma la Karonga, wauza Uchikumbe kuti mavuto odza ndi kusintha kwa nyengo atha kuchepa alimi ambiri atayamba kupanga akalozera m’minda mwawo.

Mlangiziyu adati akalozera amathandiza alimi kukolola madzi a mvula, komanso kuteteza nthaka kuti isakokololoke m’munda mwawo.

Alimi kupanga akalozera pogwiritsa ntchito chingwe

Akalozera ndi muuni wa kayendedwe ka madzi m’munda ndipo alimi amayenera kuunga mizere. Umu ndi momwe mumalimidwa milambala, yoongoledwa bwino, yomwe imachengeta nthaka podekhetsa madzi m’mizere.

“Kulima mwa chisawawa, opanda akalozera, zikuchititsa kuti nthaka izikokoloka ndi madzi a mvula.

“Zotsatira zake ndi njala chifukwa chajira chikukokoloka kusiya minda yoguga ndipo mbewu zikumauma posowa chinyezi popeza madzi amangothamangira ku mitsinje,” adatero Munthali.

Katswiriyu adalangiza alimi kupeza thandizo la alangizi a m’madera mwawo popanga akalozera.

“Osangokhala kumadikira mvula igwe mu October kapena November. Pakadalipano, mlimi wotsogola akupanga akalozera, manyowa ndi galauza,” iye adatero.

Mlangizi wina wa ku Chingale EPA m’boma la Zomba, Limbani Thangata, akuti nthaka ndi yofunika kwambiri pa ulimi choncho iyenera kutetezedwa.

“Alimi asaiwale kuti kusintha kwa nyengo kukusokoneza ntchito yathu choncho tiyenera kupanga akalozera m’munda mwawo.

“Dongosololi limathandiza kusamalira chajira poimitsa madzi n’kusunga chinyezi kwa nthawi yaitali chothandiza mbewu kuchita bwino ngakhale mvula idule,” adatero Thangata.

Mkuluyu adati kupanga akalozera ndi njira imodzi yothana ndi ng’amba kaamba koti madzi samathamanga ndipo akhala ndi nthawi yolowa pansi m’munda makamaka alimi akapanga maswale, ulimi wa m’maenje, phimbira ndi ngonyeka (box ridges).

Popanga akalozera, Thangata adati pamafunika anthu atatu, chingwe chotalika mamita 5, mitengo (ndodo) iwiri yoongoka bwino n’kutalika mamita 1.6 mpaka 2.0, chikwanje, zikhomo, hamala ndi levulo—ija amagwiritsa ntchito amisili pomanga nyumba.

Adafotokoza kachitidwe kake motere: “Anthu awiri amaima ndi ndodo zomangidwa chigwecho ndipo m’modzi amakhala pakati ndi levulo ija kuyeza. Pomwe timadzi mu levuloyo tabwera pakatikati, wa kumapeto amakhoma chikhomo ndi kusunthira komwe kuli ndime.

“Amatero mpaka kumaliza munda wonse. Malingana ndi kutsika kwa malo, akalozera amatalikirana mamita 5 kapena 10. Umu ndi momwe timaungamo milambala ija.”

M’modzi mwa alimi m’minda mwawo muli akalozera m’mudzi mwa Giliya kwa mfumu Mwaulambo m’boma la Karonga,

Jimmy Mwakila ndi mmodzi mwa alimi womwe amapanga akalozera munda mwake. Mwakila, wa m’mudzi mwa Giliya m’dera la mfumu Mwaulambo ku Karonga, adati dongosololi lamuthandiza kuti azikolola dzinthu zambiri.

“Ubwino wake wa akalozera ndi woti umapanga kamodzi basi bola osaphwasula mizere polima. Polimbikitsa milambala, ndidabzalamo udzu wa vetiva. Mlimi ofuna kusimba lokoma chaka chino apange akalozera basi,” adatero Mwakila. n

Previous Post

Quota or equitable system as a campaign issue

Next Post

Patience has its limits

Related Posts

Nkhani

 Ma rodibuloku abwerere

September 29, 2023
To be buried on Wednesday: Tembo
Nkhani

A Tembo asiya Amalawi m’misozi

September 29, 2023
Nkhani

 Liwu la mafumu pa zochotsa anthu 1 miliyoni mu AIP

September 23, 2023
Next Post

Patience has its limits

Opinions and Columns

My Turn

Don’t just ban summer classes

October 4, 2023
My Turn

Debt relief is key, but…

October 2, 2023
Guest Spot

Maneb prides over four yearsof curbing exam leakages

October 1, 2023
My Turn

Unpacking street language

September 29, 2023

Trending Stories

  • Motorists queue for scarce petrol at Crossroads Puma in Lilongwe

    Petrol crisis turns ugly

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Forgotten air Malawi tragedy

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tourism players get recognition

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi unveils inaugural electric vehicle, Citroen e-C3

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi secures K1.2BN market in china—MITC

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2023 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.