Saturday, September 23, 2023
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Nkhondo ilipo mu afcon

by Bobby Kabango
13/09/2014
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email
Atusaye (kumanja) kuthambitsana ndi mnyamata wa Ethiopia
Atusaye (kumanja) kuthambitsana ndi mnyamata wa Ethiopia

Kuphedwa kwa Ethiopia Lachitatu pa Kamuzu Stadium ndi Malawi komanso kuphedwa kwa Mali tsiku lomwelo ndi Algeria zikusonyeza kuti m’gulu B momwe muli matimu anayiwa mukhala ntchito yosayamba.

Tikukambamu timu iliyonse yasewera mipira iwiri, umodzi pakhomo ndi umodzi koyenda koma Algeria ndiyo yachita chamuna chifukwa yapambana onse.

Mali ndi Malawi ndiwo akusetekera pakamwa ngakhale sanadye mokwanira kutsatira kutolera mapointi atatu pamasewero awiri.

Mali idapha Malawi pakwawo 2-0 nkukagonja m’manja mwa Algeria 1-0 koyenda. Malawi idakwapula Ethiopia 3-2 nkugonja kwa Mali pamene Algeria yathambitsa Ethiopia 2-1 komanso Mali.

M’gululi ikutsogola ndi Algeria kutsatirana ndi Mali ngakhale ili ndi mapointi atatu chimodzimodzi Malawi koma iyo yachinyitsa chigoli chimodzi pamene Malawi yachinyitsa zigoli 4. Kumbuyo kuli Ethiopia yomwe sidatole pointi ngakhale imodzi.

Mumpikisano wa Afcon matimu awiri m’gulu lililonse amene achita bwino ndiwo amapitirira kukapikisana nawo. Apa zikusonyeza kuti masewero onse akatha woyamba ndi wachiwiri adzapita ku Morocco chaka chikubwerachi.

Mpikisanowu ukatha, timu imodzi yomwe yathera pa nambala 3 koma yasewera bwino kuposa matimu onse amene sadachite bwino idzasankhidwa kuti ipite nawo ku Morocco.

Nkhondo m’gulu B ikuoneka ikhala pakati pa Mali ndi Malawi kuti apitirire Algeria yomwe yathobola kale ngakhale Ethiopianso ili ndi mwayi wochita bwino.

Malawi pa 11 October ikulandira Algeria, timu yomwe adayigonjetsa 3-1 mu 2010. Masewerowa ali pa Kamuzu Stadium ndipo Lachitatu lake pa 15 Malawi idzatsatira Algeria m’dziko lawo kukaphana. Timu ya Algeria idakhalapo katswiri wa mpikisanowu mu 1990 itaphwasula Nigeria.

Kuti Malawi ichite bwino ikuyenera ithethetse Algeria pamene ikubwera pa Kamuzu Stadium komanso kudzapha Mali imene idzafike pa Kamuzu Stadium pa 15 November komanso iyesetse kutidzimula pakati pa Ethiopia kapena Algeria kwawo kapena pakavuta kukangolepherana nawo.

Padakalipano, timu iliyonse m’gululi ili ndi mwayi wopita ku Morocco ngati ingasamale ndi magemu akudzawa.

Masewero a Malawi ndi Ethiopia, adachinya zigoli za Malawi adali Atusaye Nyondo ziwiri ndi Frank Banda, pamene Ethiopia adayichinyira adali Getaneh Kebede ndi Yusuf Saleh.

Previous Post

A President who governs by vengeance

Next Post

‘Mavuto a kusowa zipatala anyanya’

Related Posts

Nkhani

 Liwu la mafumu pa zochotsa anthu 1 miliyoni mu AIP

September 23, 2023
Nkhani

Boma likugwiritsa K3 biliyoni pothandiza ochotsa mimba

September 23, 2023
Gogo Chabwera
Nkhani

Gogo athawa m’mudzi mwake

September 17, 2023
Next Post
Older people have always been placed at the bottom of the list when it comes to both government aid policies and programmes and those implemented by international development organisations: Old lady going to the hospital

‘Mavuto a kusowa zipatala anyanya’

Opinions and Columns

Analysis

Integrating local leaders innatural resource management

September 23, 2023
Guest Spot

Chreaa fights for OneStop Centres funding

September 23, 2023
Family Table Talk

Parenting Our Children Through Academic Failure

September 23, 2023
Layman's Reflection

Government should focus on groundwork to unlock FDI

September 23, 2023

Trending Stories

  • Unwell and without support: Chaona

    Ex-diplomats left destitute

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi passes IMF test, to get $174m

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • How others see Malawi’s tourism potential

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • DPP, ACB working to revoke Mphwiyo’s bail

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Macra in DG’s vehicle mispropcurement deal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2023 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.