Monday, August 15, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Anatchereza

by ANATCHEZERA
06/09/2020
in Chichewa
4 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Akufuna mwana

Gogo,

Ndakhala m’banja ndi mwamuna wanga zaka zisanu, koma wopanda mwana.

Mwamuna wanga amalimbitsa mtima kuti ndisadandaule popeza mwana ndi mphatso yochokera kwa Mulungu, koma abale ake ndi anga sakuimva. Akundivutitsa akuti akufuna mwana.

Nthawi zina akwawo amabwera kudzandiuza kuti ndichoke pakhomopo chifukwa ndilibe phindu.

Nditani?

HGP

 HGP,

Ndiyamike mwamuna wanu kaamba koti ndi munthu wokoma mtima, komanso wachikondi.

Akadakhala amuna ena akadakuvutitsani.

Ndigwirizane ndi mwamuna wanu kuti mwana ndi mphatso ndipo Mulungu amapereka mu nthawi yake osati yathu. Choncho abale a mwamuna wanu ndi abale anu akulakwa kumavutitsani.

Nanga akudziwa bwanji kuti vuto ndinu?

Ndikufuna ndikupempheni kuchita zinthu zitatu. Choyamba, pitani ku chipatala mukawafotokozere vuto lanu.

Chachiwiri, limbani mtima. M’moyo wathu timakumana ndi mavuto osiyanasiyana, koma timayenera kulimba mtima.

Chachitatu, mufunseni Ambuye kuti alowerere pa vuto lanu.

Natchereza

 Akundikana

Gogo,

Ndakhala ndikumufunsira mtsikana wina kwa zaka zitatu tsopano, koma amangondiyankha pompopompo kuti sakundifuna.

Poyamba ndimaona ngati ndimomwe atsikana amachitira mnyamata akawafunsira, koma panopa ndayamba kuda nkhwawa.

Nditani?

BNM

 BNM,

Fupa lokakamiza silichedwa kuswa mphika.

Ngati mtsikanayo akukukanani kuti sakukufunani musamukakamize. Musiyeni.

Mwina mukadakhala ndi chiyembekezo akadakuuzani kuti mumudikire aganize kale, koma kukuyankhani pompopompo kuti sakufuna sikukupereka chiyembekezo chilichonse.

Musadandaule, mudzapeza mtsikana wina wokukondani.

Natchereza

Akuchita nsanje

Gogo,

Mtsikana wina ndinamufunsira ndipo anandikana, koma nditapeza mnzake adandilembera kalata yokhumudwa.

Adandiuza kuti ndimusiye mtsikana winayo ndipange chibwenzi ndi iyeyo.

Ndithandizeni.

DPK

 DPK,

Musalole. Adakukanani ndipo inu mudalimba mtima ndi kupeza mnzake. Nanga akufunanso chiyani?

Musalole kulakwira mtsikana winayo poonetsa kukhulupirika kwa mtsikana amene adakukanani kale ubwenzi.

Natchereza

 Ndikufuna mkazi

Gogo,

Ndine mnyamata wa zaka 26 ndipo ndikufuna mkazi woti ndimange naye banja.

Mkaziyu akhale woti sanaberekepo, komanso wa zaka zosaposa 25.

Ine ndikukhala ku Area 25 mu mzinda wa Lilongwe ndipo amene ali wokonzeka kulowa m’banja ayimbe 0990 920 810.

PPK,

Lilongwe

Previous Post

How a senior chief succumbed to Covid-19

Next Post

Juwa bemoans absence of recognition of written poetry

Related Posts

Patrick sakubwerera mmbuyo pa chikopa
Nkhani

Patrick Mwaungulu ndi katakwe pokankha chikopa

July 24, 2022
Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Next Post

Juwa bemoans absence of recognition of written poetry

Opinions and Columns

My Turn

Making briquettes at Malasha

August 15, 2022
Candid Talk

When parents demand more

August 14, 2022
People’s Tribunal

Time is not on the side of PDP

August 14, 2022
Big Man Wamkulu

She is very elusive, loves money

August 14, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • World Bank suggests kwacha re-alignment

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • AG wants Chisale’s K3.4bn claim axed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • UDF fills up positions

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Agriculture, education reforms on rocks

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tadala kandulu ngosi: Malawi open champion tennis genius 

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.