Nkhani

Banda adataya mwayi

Listen to this article

Mtsogoleri wa dziko lino Joyce Banda  adataya mwayi wosonyeza bwino lomwe kuti akudziwa chimene akuchita polimbana ndi  chiwanda chidalowa kulikulu la dziko lino kumene ogwira ntchito m’boma agundika  kupakula ndalama.

Mmalo monena zimene akuchita, iye  adataya nthawi yaitali kunena kuti kubako kudayamba zaka 20 zapitazo.  Atolankhani ena atamufunsanso ngati achotse nduna ya zachuma, oyendetsa chuma  cha boma komanso mlembi wamkulu mu ofesi ya pulezidenti ndi nduna zake, iye  adati sangatero.

M’mbuyomu, Banda adaneneratu kuti  adadziwa za kupakula kumene kumachitikako miyezi isanu yapitayo. Tsono tikudabwa  kuti atazindikira adachitapo chiyani? Nanga n’chifukwa chiyani palibe chimene  amachita kufikira mkulu woyendetsa ndondomeko ya zachuma Paul Mphwiyo  adaomberedwa?

Kunena kuti sangachotse ntchito  akuluakuluwo kukusonyeza kuti pali china chimene if sitikuuzidwa. Khoswe wakhala  pa mkhate apa. Akuluakuluwo amayenera kutula pansi maudindo awo okha, osadikira  kuchotsedwa izi zitaphulika. Chifukwa choti sadachite izi, ambiri amayembekeza  awachotsa.

Kuchotsa akuluakuluwo ndi njira imodzi  yoti kufufuza kuyende bwino.

Ndalama zimene zimaseweretsedwazo si za  Banda kapena akuluakulu a bomawo ayi. Izi ndi ndalama zimene Amalawi amakhetsera  thukuta pokhoma misonkho. Izi ndi ndalama zimene zikakadathandiza Amalawi  pachitukuko: kumanga sukulu, zipatala, kutukula ulimi ndi ntchito zina  zotere.

Related Articles

Back to top button