Nkhani

Akhapana kaamba ka ufumu ku ntchisi

Listen to this article

Anthu atatu akhapidwa mpaka kugonekedwa m’chipatala pa mkangano wa ufumu wa nyakwawa Kandanda kwa Senior Chief Kalumo m’boma la Ntchisi.

Potsimikiza nkhaniyo, a Kalumo ati mmodzi mwa okhapidwawo akuyembekezera kukadulidwa dzanja kuchipatala chachikulu cha Kamuzu Central ku Lilongwe.

Naye mneneri wapolisi ku Ntchisi a Yohane Tasowana atsimikiza zankhaniyo ndipo ati nyumba za anthu atatu omwe adakhapidwawo zidagumulidwa ndipo anthu 8 adamangidwa.

“Tamanga anthu 8 ndipo tawatsegulira milandu iwiri, woononga katundu wa eni ndi wina wovulaza anthu. Tikakonzeka tiwatengera kukhoti,” atero a Tasowana.

A Kalumo adati mkanganowo si walero udayamba kalekale kuli ufumu umodzi wokha wa a Kandanda ndipo a Njovu akhala alipansi pa a Kandandawo.

“Ufumu wa a Kandada ndi wakalekale. Nthawi yonseyi a Njovu adali pansi pa a Kandada koma kenako adayamba kuvuta,” atero a Kalumo.

Iwo ati m’zaka za mmbuyomo mkanganowo utakula, iwo adagamula kuti a Njovu akhale ndi wawo ufumu ndipo zidatheka adawaveka ufumuwo m’chaka cha 2018.

“Ndinkaona ngati kupereka ufumu wapadera kwa a Njovu kuthetsa mikanganoyo koma ayi mpomwe zankira patsogolo mpaka kufika pomatemana n’kumagumulirana nyumba,” atero a Kalumo.

Iwo ati mafumu awiriwo ndi ofanana mphamvu koma chomwe bwalo lawo likuona nchoti mtima wa a Njovu umawawa chifukwa salandira mswahara pomwe anzawo a Kandanda amalandira mswahara.

“A Njovu akuvuta kuti ufumu wa a Kandanda utheretu ndipo iwowo ndiwo akhale a mfumu ndiye tikudabwa kuti kodi akufuna ufumuwo kapena nkhani ndi mswahara,” atero a Kalumo.

Iwo ati potsatira mwambo wa ufumuwo, a Kandanda ndiye eni ufumu chifukwa nkwa mayi awo pomwe a Njovu nkwa abambo awo ndipo ufumuwo munthu amakalowa kwa mayi ake.

Mkulu woyang’anira za mafumu ku unduna owona za maboma aang’ono a Charles Makanga ati nkhaniyo ndi yofunika pakhonsolo chifukwa maufumuwo ndi wosankhidwa komweko.

“Unduna umalowelera ufumu wosankhidwa ndi apulezidenti koma wosankhidwa pa khonsolo umathera pakhonsolo pomwepo,” adatero a Makanga.

Uwu ndi mkangano wa ufumu wachiwiri wawukulu chaka chino chokha chifukwa kumayambiliro padalinso mkangano wolimbirana ufumu wa Chikulamayembe m’boma la Rumphi.

Mkangano wa ufumu wa a Chikulamayembe udafika povuta kwambiri mpaka gulu lotsutsana ndi yemwe adavekedwa ufumuwo adagenda galimoto zaboma tsiku lomwe apulezidenti a Lazarus Chakwera adapita kukaveka ufumuwo.

Related Articles

Back to top button
Translate »