Tuesday, August 9, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Mkulu wa zaka 22 akaseweza zaka 23

by Bobby Kabango
31/07/2015
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Wakhala akuthyola nyumba masana kasanu konse ndi kubamo katundu. Anthu ku Balaka akhala akumusaka koma adali woterera ngati mlamba. Koma la 40 lamukwanira John Bunaya, wa zaka 22, amene bwalo la milandu lamuthowa ndi zaka 23 kuti akaseweze kundende chifukwa cha kutolatola.

Wapolisi woimira boma pamilandu, Inspector Isaac Mponela, wati bwalo la Balaka lidapeza mkuluyu wolakwa pamilandu yonse isanu yomwe adapalamula.arrest

Mponela adauza bwalolo kuti pa 3 March, chaka chino, masanasana dzuwa likuswa mtengo, Bunaya adaswa nyumba ya Gloria Mphwiyo ndi kubamo njinga ya komanso matumba awiri a chimanga. Zonse zidali za mtengo wa K43 000.

Pa 28 March, chaka chonchino, Bunaya akutinso masanasana adaswa nyumba ya Ruth Marley ku Majiga m’bomalo ndi kubamo wailesi komaso zovala ndi katundu wina.

Bunaya pa 13 April, akuti adaphwanyanso nyumba ya Rachel Jika ndi kubamo laputopu, matilesi, mafuta ophikira ndi shuga za K320 000.

Pa 10 May, Bunaya akuti adaswa nyumba ya William Munthali ndi kubamo kamera, foni ndi zakugolosale za K72 000.

Iye sadalekere pomwepo. Pa 13 May akuti njondayi idakaswanso nyumba ya Daniel Pondani komwe adakasokolotsa DVD, masipika awiri a LG, mafuta ophikira ndi mafoni za K100 000.

Mponela atamaliza kumunenera Bunaya kubwaloko, anthu adadzidzimuka. Izi zidadabwitsanso woweruza milandu, Victor Sibu, yemwe sadachedwe koma kusatakula chilango chokhwima.

Iye adalamula Bunaya, yemwe adavomera kulakwa pamilandu yonseyi, kuti akaseweze zaka 23 ngakhale iye adaliralira kuti ndi wachichepere komanso ndiye amasamala banja lake ndi makolo omwe adati ndi okalamba.

Bunaya amachokera m’mudzi mwa Kandengwe kwa T/A Nsamala m’bomalo.

Previous Post

Zavutanso ku Mozambique

Next Post

Utsi ku Nam pamene ma Queens anyamuka

Related Posts

Patrick sakubwerera mmbuyo pa chikopa
Nkhani

Patrick Mwaungulu ndi katakwe pokankha chikopa

July 24, 2022
Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Next Post

Utsi ku Nam pamene ma Queens anyamuka

Opinions and Columns

My Turn

Bitcoin and regulations

August 8, 2022
Editor's Note

My beautiful experience as an intern

August 7, 2022
Editor's Note

My beautiful experience as an intern

August 7, 2022
Big Man Wamkulu

What is he up to? He doesn’t drink

August 7, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Macra ordered MultiChoice Malawi not to 
implement the new proposed tariffs

    Court rebuffs MultiChoice Malawi on new tariffs

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Treasury Secretary says won’t resign

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Judiciary under probe 

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chakwera’s austerity measures questioned

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Rip-off 

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.