Nkhani

Nam yapindulanji pa Tigresses?

Bungwe la Malawi National Council of  Sports tsopano layeretsa timu ya Tigresses kuti Nam ndiyo yolakwa pankhani yoti  timuyi ichotsedwe m’chikho cha Presidential Initiative for Sports chifukwa  idaseweretsa wotupa mchombo.

Tithokoze kuti chilungamo chadziwika  ndipo timuyi ipikisanabe m’chikho cha apulezidenti.

Tilangizeko Nam kuti sibwino kuchita  zinthu mwa nkhwidzi, zigamulo zinazi tiyeni tizilowa mmalamulo chifukwa  zikusokoneza.

Taonani chikho cha apulezidenti  chidayima pamene timati tikupseda. Onaninso kuti osewera a timuyi asiyidwa ku  Australia. Ndalama zawonongeka komanso mwasokoneza timu ya dziko  lino.

Nam sibwino kumaonetsa poyera matimu  amene mumakwera. Kukhala ndi timu yapamtima sikoletsedwa koma zimafunika kuti  matimu onse azithandizidwa mofanana.

Zotere musadzachitenso, aka kakhale  komaliza. Pajatu timuyi ili panambala yoyamba mu Africa muno ndiye sitikufuna  ichoke pamenepo. Mwaphunzirapo kanthu chonde sinthani kusanade.

Tifunire zabwino zonse timu ya dziko  lino yomwe ili m’dziko la Australia kukapikisana ndi matimu ena anayi. Mary Waya  ndi Griffin Saenda gwirani ntchito ndi osewera 12 mwatengawo ndipo ife  tikuyembekezera zabwino.

Aganyu m’sabatayi timakambirana za  mphunzitsi wabwino m’dziko muno. Zikuonetsa kuti aphunzitsi odziwa ntchito alipo  amene mwina utawapatsa mwayi atha kunyamula Flames.

Aganyu ambiri akukambabe za mphunzitsi  wakale Kinnah Phiri kuti ndiye wabwino. Ena akukamba za Elijah Kananji wa  Blantyre United. Pamene Fam ikusakasaka mphunzitsi wa Flames, chonde tawunguzani  m’dziko muno.

Related Articles

Back to top button