Nkhani

Sinodi ya Nkhoma ikudana ndi zochotsa mimba

Listen to this article
Asadzasainire: Banda
Asadzasainire: Banda

Sinodi ya Nkhoma ya mpingo wa CCAP yati kuloleza kuti amayi azichotsa mimba ndi kolakwika, nkhanza, uchimo komanso usatana pamaso pa Mulungu chifukwa ndi kuchotsa moyo wa munthu.

Zonena za mpingowu zadza pamene mtsutso ukukula kuti malamulo a dziko lino asinthidwe kuti amayi azichotsa mimba ngati angafune. Padakali pano, malamulo a dziko lino amaletseratu kuchotsa mimba kupatula pomwe madotolo atanena kuti kusunga mimbayo kuika moyo wa mayi kapena mwana yemwe akuyembekezera uli pachiopsezo.

Chikalata cha mpingowo chimene adachisayina mbusa Vasco Kachipapa komanso mbusa Brian Kamwendo chidati moyo umayambika pamene mphamvu ya bambo ndi ya mayi zikumana n’kupanga mwana ndipo imapitirira nthawi yonse imene mayi ali ndi mimba mpaka mwana kubadwa, kukula mpaka kufa kapena kumwalira.

“Choncho kuchotsa pathupi n’kulakwira malembo oyera,” chikalatacho chidatero.

Padakali pano, bungwe lounikira malamulo la Malawi Law Commission likukonza bilo yokhudza zochotsa mimba, ndipo ngati biloyo aphungu a ku Nyumba ya Malamulo atakaivomereza, idzakhala lamulo lololeza kuchotsa mimba.

Koma chikalatacho chidati aphungu asakalole izi chifukwa adasankhidwa kuti ateteze miyoyo ya anthu.

“Tikupemphanso mtsogoleri wa dziko lino Joyce Banda, yemwe ndi mzimayi kuti ngati aphungu angaloleze lamulolo, iye adzakane kusainira kuti zitero,” chidatero chikalatacho.

Unduna wa zaumoyo wati kuchotsa mimba kumadzetsa mavuto ena ndipo boma limaononga K300 miliyoni chaka chilichonse pothandiza amayi amene adakachotsa mimba mobisa pogwiritsa ntchito njira zodziwa okha.

Related Articles

One Comment

  1. A Nkhoma Synod asiye kulowelera pa nkhani yomwe sikuwakhuza. Palibe yemwe amayitana a tchalitchi pamene akutenga mimba ndipo a tchalitchi sasamala mimba angakhale kupeleka chisamalo cha mwana/ana. A tchalitchi nkhaniyi sikuwakhuza iwo ntchito yawo ndikulalikira basi. Kuonjeza apo, amuna amathawa mimba nthawi zonse opanda kuthandiza angakhale pang’ono – nthawi yakwana yoti amayi ndi atsikana akhale ndi ufulu wosankha ngati akufuna kusunga mimba kapena kuichotsa. Ndi ufulu wa amayi kutero monga mmene kwa nthawi yayitali abambo akhala ndi ufulu wothawa mimba ndi kusamalira ana. Dziko lathu likhala ndi chiwelengero chabwino komanso atsikana atha kupitiliza sukulu opanda kupatsa chiphinjo chosiira mwana wawo ndi makolo kapena abale.Ngati atchilitchi akufuna kuchotsa zinthu zodzetsa machimo bwanji achite BAN mowa etc.

Back to top button