Saturday, August 20, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Tikolola chimanga chochuluka—Nduna

by Staff Writer
13/04/2013
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Nduna ya zamalimidwe komanso kuonetsetsa kuti m’dziko muno muli chakudya chokwanira, Peter Mwanza yati undunawu ukulosera kuti chaka chino dziko lino likolola chimanga chochuluka ndikukhala ndi china chapadera.

Polankhula Lachitatu mumzinda wa Lilongwe pomwe amafotokozera atolankhani za kholola wa chaka chino, ndunayi yati malinga ndi zolosera dziko lino lingapate matani 740 000 a chimanga apadera. Chaka chatha dziko lino lidapeza matani oposa 500 000 apamwamba.

Zolosera za ndunayi zikudza pomwe zadziwika kuti Dedza ndi madera ena kuchigawo cha kumpoto kwa dziko lino mvula yachita njomba ndipo alimi ali pachiopsezo kuti mwina galu wakuda awayendera kumeneko.

Ngati zoloserazo zingatheke ndiye kuti dziko lino likhala ndi chakudya chambiri chapadera chifukwa dziko lino limafuna matani achimanga 2.6 miliyoni.

Mwanza adati ichi ndi chisonyezo chabwino kuti dziko lino lapata chimanga chambiri chapadera ndipo adati boma liyesetsa njira ya zipangizo zotsika mtengo kuti dziko lino lipate chakudya chambiri.

Mtsogoleri wa dziko lino, Joyce Banda polankhula atangokwanitsa chaka akulamulira ku Lilongwe adati madera omwe akhudzidwa ndi njala ndi ochepa kotero boma liyesetsa kuti ulimi wa mthirira uyambike kuti njala ithe m’dziko lino.

Mu 2012 dziko lino lidapeza matani 3.624 miliyoni a chimanga ndipo chapadera adali matani 566 552 pomwe mu 2011 tidakolola matani 3.8 miliyoni ndi chapadera matani 1.2 miliyoni.

Padakali pano boma kudzera mwa Banda lalengeza kale kuti ndondomeko ya makuponi ipitirira ndipo anthu omwe adzalandire makuponiwa ndi 1.5 miliyoni. Nambalayi idakwezedwa pomwe Banda adayamba kulamula kuchoka pa 1.4 miliyoni.

Previous Post

NPL online editor Liz Banda dies

Next Post

JB’s gender was irrelevant, so is Atupele’s age

Related Posts

Patrick sakubwerera mmbuyo pa chikopa
Nkhani

Patrick Mwaungulu ndi katakwe pokankha chikopa

July 24, 2022
Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Next Post

JB’s gender was irrelevant, so is Atupele’s age

Opinions and Columns

My Turn

Diagnostic tech cost on patients

August 19, 2022
Business Unpacked

Why public debt should worry every patriotic Malawian

August 18, 2022
Rise and Shine

How to triumph in interviews

August 18, 2022
My Turn

Making briquettes at Malasha

August 15, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Challenged the sale: Chakaka-Nyirenda

    Court nods to transfer of bus depots

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • 3 prisoners ‘forgotten’ on death row

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Court reinstates Namalomba in PAC role

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • My dad is proud—Daliso 

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Ecobank Malawi rolls out new digital promotion

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.