Tuesday, August 9, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Agulitsa mwana ndi K18 miliyoni

by Martha Chirambo
26/02/2022
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Nkhondo ndi anansi. Wodya naye mbale imodzi ndiye amakupereka kwa adani. Izi zapherezera kwa mwana wina wa zaka 11 yemwe msuweni wake anamutsatsa pa mtengo wa K18 miliyoni.

A Madalitso Wyson, yemwe ali ndi zaka 22, adapita kusukulu kwa mwanayu ku Chingazi, m’dera la Ntambanyama m’boma la Thyolo pa nthawi yopuma ndi kumutenga mwanayo. Apolisi m’boma la Thyolo atsimikiza za nkhaniyi.

Malinga ndi mneneri wa polisi m’bomalo a Amos Tione, a Wyson atamutenga mwanayo yemwe ali m’sitandade 2, adapita naye kwa chibwenzi chake komwe anakagona kwa tsiku limodzi.

“Zonsezi zimachitika makolo a mwanayo asakudziwa kanthu,” anatero Tione.

Iwo adati kutacha m’mawa, Wyson adamutenga mwanayo kupita naye pamsika wa Ntambanyama pomwe anakakumana ndi sing’anga wina ndi kumutsatsa malondawo.

“Koma sing’angayo anatsina khutu anthu ena komanso apolisi ndipo a Wyson adatsekeredwa pamlandu wozembetsa ana mosemphana ndi gawo 15 la malamulo wozembetsa anthu,” adatero a Tione.

Msangulutso udacheza ndi sing’anga Billy yemwe anati zokambirana zake ndi Wyson zidaonetsa kuti munthu yemwe mnyamatayo anapangana naye kugula mwanayo anamugwiritsa fuwa lamoto.

Billy adati Wyson atafika pamalo ake a ntchito anamuitanira pambali n’kumuuza kuti pali bizinesi ya mwanayo.

“Adandiuza kuti adapangakonso bizinesiyi mmbuyomo ndi anzake omwe adamupusitsa ndi kuthawa ndi ndalama, ndipo ulendo uno adaganiza zochita bizinesiyo yekha,” adatero a Billy.

Iwo adati Wyson adawauzanso kuti ngati akufuna akhoza kumupatsa wokonzakonza.

“Pofuna kupulumutsa moyo wa mwanayo, ndidamuyenda pansi ndi kupeza mkulu wina yemwe adanamizira ngati wogula kwinaku ndikuimbira foni apolisi omwe adadzamumanga,” adatero a Billy.

Iwo adati aka si koyamba chifukwa mmbuyomu adafikiridwakonso ndi anthu ena omwe adawauza kuti akufuna chizude pa mtengo wa K10 miliyoni ndipo adazindikira kuti iyi inali njira yongozembaitsa chifukwa anthuwo amafuna munthu.

Ndipo mkulu woyang’anira maphunziro m’boma la Thyolo a Godfrey Kubwense adatsimikiza kuti mphunzitsi wamkulu wa pasukulu ya Chingazi adawadziwitsa za nkhani ya mwanayo.

Nkhani zozembetsa anthu zakhala zikukula m’dziko muno. M’chaka cha 2020 anthu 688 adapulumutsidwa ku mchitidwewu.

Previous Post

Elizabeth Bandason: Shaping the future of farming with science

Next Post

Players union faults Bullets over contracts

Related Posts

Patrick sakubwerera mmbuyo pa chikopa
Nkhani

Patrick Mwaungulu ndi katakwe pokankha chikopa

July 24, 2022
Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Next Post
Nyirenda: The door
is open

Players union faults Bullets over contracts

Opinions and Columns

My Turn

Bitcoin and regulations

August 8, 2022
Editor's Note

My beautiful experience as an intern

August 7, 2022
Editor's Note

My beautiful experience as an intern

August 7, 2022
Big Man Wamkulu

What is he up to? He doesn’t drink

August 7, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Macra ordered MultiChoice Malawi not to 
implement the new proposed tariffs

    Court rebuffs MultiChoice Malawi on new tariffs

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Treasury Secretary says won’t resign

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Judiciary under probe 

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chakwera’s austerity measures questioned

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Nankhumwa rally irks DPP governor

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.