Wednesday, October 4, 2023
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Apolisi amanga mayi wa mwana womwa kachasu

by Martha Chirambo
06/10/2019
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Apolisi ku Chirimba mu mzinda wa Blantyre akwizinga mayi wa mwana ndi anzake awiri powaganizira kuti amalekerera ndi kuyamikira mwana wa zaka zinayi akugwetsa matoti a kachasu.

Amayiwa adawamanga potsatira kanema yemwe amazungulira pa masamba a mchezo a Facebook ndi WhatsApp yoonetsa mwanayu akupapira kachasuyo.

An illustration of an arrest

M’malo momuletsa, amayiwa akuwaganizira kuti amamuchemerera mwanayo kwinaku akumufunsa mafunso n’kumamujambula kanemayo.

Kanemayu akuonetsa mwana akugwetsa matoti a kachasu ngati akumwa madzi kwinaku akufotokoza kuti adamuphunzitsa kupapira kachasu ndi azakhali ake aku Ndirande.

Mwanayu adagwetsa yekha botolo la kachasu la mamililita 250.

Mneneri wa polisi wa ku Blantyre, Augustus Nkhwazi, wauza Msangulutso kuti amayiwa adakaonekera ku khoti Lachitatu pa October 2 pa mlandu wochita chikhalidwe choononga ( harmful cultural practices) womwe umapezeka m’gawo 80  la malamulo oteteza ana a m’dziko muno.

Nkhwazi adati khoti latulutsa amayiwa pa belo atapereka chikole cha K40 000 aliyense.

“Koma pakadali pano  mwanayu ali m’manja mwa agogo ake mpaka mlanduwu udzathe. Akhoti adauzanso a nthambi yoona zakasamalidwe ka ana m’dziko muno kuti apeze malo wokasungirako mwanayu pa nthawi ya mlanduwu,” adalongosola Nkhwazi.

 Malipoti a ku bwalo la milandu akusonyeza kuti bambo wa mwanayu adakwiya ndi kanemayo mpaka adakasumira ku khoti amayiwo.

 Amayiwa aukana mlanduwo ndipo khoti layamba kaye laimitsa mlanduwu mpaka pa October 22 2019.

Bungwe lomenyera ufulu wa ana la Centre for Human Rights Education Advice and Assistance (Chreaa) lati ndi lokhumudwa ndi nkhaniyi.

Chaguluka Mhango, m’modzi mwa ogwira ntchito ku Chreaa, adati: “Amayiwa amadziwa kuti mwanayu akulakwitsa ndipo amayenera kumuletsa.

“Koma m’malo motero amajambula kanemayo ndi mwansangala. Apatu zikuonetseratu kuti malo womwe mwanayu akukulira siwoyenera mwana kukhalapo.”

Iye adati pakadali pano mwanayu akufunika thandizo chifukwa kachasu ndi wa mphamvu wosayenera ana kumwa. n

Previous Post

Long walk to fighting breast cancer

Next Post

Mulli denies receiving money from govt

Related Posts

Nkhani

 Ma rodibuloku abwerere

September 29, 2023
To be buried on Wednesday: Tembo
Nkhani

A Tembo asiya Amalawi m’misozi

September 29, 2023
Nkhani

 Liwu la mafumu pa zochotsa anthu 1 miliyoni mu AIP

September 23, 2023
Next Post

Mulli denies receiving money from govt

Opinions and Columns

My Turn

Don’t just ban summer classes

October 4, 2023
My Turn

Debt relief is key, but…

October 2, 2023
Guest Spot

Maneb prides over four yearsof curbing exam leakages

October 1, 2023
My Turn

Unpacking street language

September 29, 2023

Trending Stories

  • Motorists queue for scarce petrol at Crossroads Puma in Lilongwe

    Petrol crisis turns ugly

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Forgotten air Malawi tragedy

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tourism players get recognition

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi unveils inaugural electric vehicle, Citroen e-C3

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi secures K1.2BN market in china—MITC

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2023 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.