Nkhani

Kodi za Gaba zalowa?

Listen to this article

M’sabatayi aganyu tidali osangalala kumva kuti chilombo cha ukonde, Gabadihno Mhango, mwana wa Flames, tsopano wayamba kusewerera m’timu yatsopano ya Bloemfontein Celtic.

Kuonetsa ukadaulo wake, chilombochi chidathandiza timuyi pofanana mphamvu ndi Moroka Swallows, pomwe masewerowo adathera 2-2 Gaba atachinya patangotsala mphindi ziwiri kuti masewero athe.

Kumeneku ndiye timati kubwera, ngakhale zina zimavuta mwanayu amatha kuwona ukonde.

Komabe tati tifunse ngati ndalama za mnyamatayu zalowa. Mmene adasewerera patsikuli zidaonetsa kuti sadapite pamtengo wolira.

Zimasonyezeratu kuti kukatamuka kulipo zikangolowa. Kodi zalowa zingati? Ena alankhulapo kuti popeza Gaba adapita monga wopanda timu ndiye kuti apita wabule.

Tikukhulupirira kuti awa ndi mabodza, paja Amalawi amakonda kumva zamabodza. Tikuyembekeza kuti zikalowa zinthu zisintha kukalabu.

 

Za bolera zili pati?

Moni kwa Nyerere, Jombo ya KB, Mabankers komanso Civo pamene ntchito ikuyambika lero ku Lilongwe m’chikho cha Standard Bank. Ena atuluka mmawa weniweni kuli mbuuu!

Komabe izo zili apo, aganyu tafuna timve za momwe bolera wotchedwa Solomon akupezera.

Mnyamata ameneyu adapondedwa ndi jombo mwezi wathawu koma kufika lero sizikudziwika momwe akupezera.

Aliyense wangoti ziii, kapena ndi zopanda ntchito? Malipoti akungoti wasiya kulankhula, ena ati wasiya kupita kusukulu. Monga aganyu tati tifuseko a Sulom kuti kodi munamuyendera mnyamatayu? Nanga ali bwanji?

Related Articles

One Comment

  1. My dear freind, I would like to comment on the issue u wrote in nation nwspaper of 2 november 2013, just to remind u, u asked that WHY ARE THE POLICE FAILING TO ARREST PEOPLE WHO STARTS VIOLENCE IN THEIR PRESENTS? MAY BE ISNT A PROBLEM TO START VIOLENCE IN FOOTBALL STADIUM. I also heard u say POLICE ARE THE ONE TO BLAME. My dear friend, some where ur right but somewhere ur wrong, am a police officer from Balaka. Observation has shown that most super league sulom/fam hires 10 police officers, CAN 10 POLICE OFFICERS MANAGE TO HANDLE A SITUATION INVOLVING OVER 10,000 PEOPLE? We ve been hired by solum here at BK police to provide security im most super league teams, most times they hires 10 police men except for wanderers and Redlions game where they hired 40 policemen, to answer ur question short, solum and fam are the ones to be blamed, once thy come to ask for police men to provide security in football matches, they always told the necessary number of police personnel to do the job bt they always come up with there number in which is 2, 4, 6, 8, 10 and very rare 15 except for that wanderes and redlions game in the standard bank cup. So look, who hires the police? Its solum and fam. Tsono apolice ndi anthunso, moyo wawo amaukonda, ndalama imene amalandila ndi k2500, kustadium kumafunika zambiri, mumagate mumafunika apolice, kumastand in both sides plus VIP stand, anthu 10 agwira bwanji ntchito? Inunso pene atolankhani be proffesional, mumapita kustadium, can u say u never observed what am saying? Why always police? Have u ever noticed violence in flames games? Ask urself why? Kumakhala more than one thousand policemen, ziwawa zingachokere kuti with such huge presents of police officers? Tithandizeni atolonkhani. I ve said this after observation and experience. If anything u can find me on facebook, search for Bro Geo Geoff Chipengule, my email adress is chipenguleb@gmail.com

Back to top button