Monday, August 15, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Tikwanitsa lonjezo lililonse—Chakwera

by Steven Pembamoyo
19/03/2021
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Mtsogoleri wadziko lino Lazarus Chakwera wati Amalawi asamvere za anthu omwe akufalitsa kuti boma lake lafotsera malonjezo omwe lidapereka pa nthawi yakampeni.

Chakwera adanena izi poyankha funso la phungu wa kumwera cha kumadzulo kwa boma la Nkhata Bay Noah Chimpeni yemwe amafuna kuti afotokoze malonjezo omwe boma lake laika patsogolo pa en. onse.

Chakwera adakayankha mafunso ku Nyumba ya Malamulo

Iye amakaonekera kachitatu ku Nyumba ya Malamulo chitengereni mpandowo kukayankha mafunso osiyanasiyana a aphungu.

Poyankha funso la Chimpeni, Chakwera adati boma la Tonse Alliance lidayamba kale kukwaniritsa malonjezo omwe adali ofunika kwambiri ndipo ena onse azikwaniritsidwa malingana ndi nthawi.

“Pasakhalenso nkhawa iliyonse yokhudza malonjezo chifukwa boma ilili likwaniritsa lonjezo lililonse lomwe lidaperekedwa koma nthawi ndiyo izinena malingananso ndi kufunika kwa lonjezolo,” adatero Chakwera.

Iye adatchula pulogalamu ya zipangizo zaulimi zotsika mtengo ya Affordable Inputs Programme (AIP), kukweza ndalama zoyambira malipiro kufika pa K50 000 komanso kuonjezera malipiro osayenera kudula msonkho kufika pa K100 000.

“Malonjezo awawa sakadadikira chifukwa akukhudza miyoyo ya Amalawi monga kukhala ndi chakudya chokwanira komanso kukhala ndi ndalama kuti moyo wawo uziyenda bwino,” adatero Chakwera.

Iye adadandaula kuti anthu ena amapupuluma kudzudzula kuti zinthu zikuchedwa kuiwala kuti zonse sizingatheke nthawi imodzi.

Mabungwe omwe siaboma akhala akudzudzula Chakwera ndi boma la Tonse Alliance kuti akuchedwa kukwaniritsa zomwe adalonjeza pa kampeni kapena kupeleka ndondomeko yamomwe bomalo likwaniritsile malonjezowo.

Mkulu wa bungwe la Centre for Democracy and Economic Development Initiative (Cdedi) Silvestre Namiwa adapempha Chakwera kuti asayiwale malonjezo omwe adamuika pampando.

“Manifesito ya Tonse Alliance idali yokopa mtima kwabasi n’chifukwa chake anthu adayivotera koma koma zikuoneka kuti adangofunako mavoti chifukwa palibe lonjezo lomwe likuwoneka,” adatero Namiwa.

Wapampando wa mgwirizano wa mabungwe oyima pawokha omwe ali pansi pa National Advocacy Platform (NAP) Benedicto Kondowe adati poyembekezera nthawi yokhazikikayo, Chakwera ndi boma lake akuyenera kufotokoza momwe malonjezowo awakwaniritsire.

“Nzoona kuti malonjezowo ndi ambiri sangakwaniritsidwe nthawi imodzi koma pofika pano akadafotokoza ndondomeko kuti adzakwaniritsa bwanji,” adatero Kondowe.

Kadaulo pa ndale George Phiri adagwirizana ndi Chakwera kuti malonjezo ena sangaoneke mmiyezi 8 yomwe iye wakhala pampando wa upulezidenti.

Previous Post

Pirates legend says Gaba is selfish

Next Post

Zokolola zichuluka

Related Posts

Patrick sakubwerera mmbuyo pa chikopa
Nkhani

Patrick Mwaungulu ndi katakwe pokankha chikopa

July 24, 2022
Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Next Post
Amalawi kulimbirana chimanga nthawi ya njala

Zokolola zichuluka

Opinions and Columns

My Turn

Making briquettes at Malasha

August 15, 2022
Candid Talk

When parents demand more

August 14, 2022
People’s Tribunal

Time is not on the side of PDP

August 14, 2022
Big Man Wamkulu

She is very elusive, loves money

August 14, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • World Bank suggests kwacha re-alignment

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • AG wants Chisale’s K3.4bn claim axed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • UDF fills up positions

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Agriculture, education reforms on rocks

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tadala kandulu ngosi: Malawi open champion tennis genius 

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.