Sunday, August 14, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Waganyu: Kulibe mipira yokonzekera zoona?

by Bobby Kabango
01/11/2014
in Nkhani
1 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Bungwe la FAM laletsa anyamata a Flames kuti asachite zokonzekera chifukwa ndalama palibe. Pofika dzulo zidali zisadadziwike ngati Malawi isewere ndi Mali komanso Ethiopia.

M’ndondomeko ya zachuma, Flames idalandira K70 miliyoni m’malo mwa K400 miliyoni. Pano ndalamayi yatha ndipo FAM palibe ingachite koma kulepheretsa zokonzekerazi.

Kodi apa tidzudzule boma kapena tiloze zala FAM? Vuto la mpira m’dziko muno si lachilendo ndipo ife sitikudzidzimuka kumva kuti boma lili chabechabe.

Misonkho yathu ikumakhala yokangobetsa osati kugwirira ntchito yomwe ifeyo tikufuna. Anthu akuzunzika kaamba kosowa mankhwala komanso zina. Apanso ndi izi kuti mpira tsopano ukupita pansi.

Masewero a mpira wamiyendowu ndiwodula kwambiri kusiyana ndi ena. Ife tikuona kuti Amalawi sitidakonzeke kuti tizipezeka nawo m’mipisano monga wa Afcon chifukwa mapeto ake tidzikhala ndi ndalama zosewerera gemu koma kulephera kupeza zokonzekera.

Sitikudziwa kuti anduna athu adziti chiyani apapa polingalira kuti adalonjeza kuti Flames ilandira ndalama zake mpaka kumaliza mpikisanowu?

Tikudabwa chifukwa tikayang’ana kuchipatala kuli mavuto, ku ulimi ndiye wosakamba, nako ku zamaphunziro ndi misewu ndiye mavuto a nkhaninkhani. Ndiye msonkho wathu uzigwira ntchito yanji?

Kapena ntchito ya misonkho yathu nchiyani? Kapena mufuna izingobedwa pamene ife tikuvutika? Ifetu zatikwana ndipo chiyembekezo chathu n’chakuti nduna ya zamasewero Grace Chiumia alankhulapo pa zomwe zikuchitikazi.

Previous Post

ACB probed Mphwiyo for Cashgate from Sept 2013

Next Post

Olumala asaiwalidwe, Fedoma yatero

Related Posts

Patrick sakubwerera mmbuyo pa chikopa
Nkhani

Patrick Mwaungulu ndi katakwe pokankha chikopa

July 24, 2022
Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Next Post

Olumala asaiwalidwe, Fedoma yatero

Opinions and Columns

Candid Talk

When parents demand more

August 14, 2022
People’s Tribunal

Time is not on the side of PDP

August 14, 2022
Big Man Wamkulu

She is very elusive, loves money

August 14, 2022
My Thought

Stop cyber harassment

August 14, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • World Bank suggests kwacha re-alignment

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  •   MPs on trial

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Mindset change should target Indian-Malawians

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Wanderers pen Sulom over refs

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Did ACB, LMC rush? 

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.