Tuesday, August 9, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Yamikani ‘Headmaster’ Fodya wa Bullets

by Bobby Kabango
26/07/2015
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Dzina la Yamikani Fodya lawanda. Uyutu ndi mnyamata wokankha chikopa kutimu ya Flames komanso ku Big Bullets. Iyeyu wapatsidwa maina osiyanasiyana kaamba ka luso lake lomwe ochemerera mpira akuliyamikira monga mwa dzina lake. BOBBY KABANGO akumva za mbiri yake.

Fodya: Mulungu akakonza palibe angatsutse
Fodya: Mulungu akakonza palibe angatsutse

Tikambire za mbiri yako…

Ndimachokera ku Balaka. Ndine wa nambala 7 kubadwa m’banja la ana 8. Ndinenso wokwatira ndipo ndili ndi mwana mmodzi dzina lake Favour.

 

Ku Bullets udabwerako liti?

Ndidafika mumzinda wa Blantyre mu 2009. Nthawiyo n’kuti kutangoyambika chikho cha Presidential Cup ndiye anthu adaona luso langa mpaka kundiitanira kutimuyi.

 

Udalandiridwa bwanji?

Kundirandira kudali bwino koma kupeza mwayi wosewera padavuta. Ndidapeza osewera ambiri, ngakhale ku training sindimapeza mwayi. Ngakhale kutulutsa timu yonseyo, mwayi wolowabe sumapezeka.

 

Nanga umasewera malo ati?

Nthawiyo ndimasewera pakati, malo amene ndimasewera ku Young Soccer ya ku Dedza.

 

Zidatani kuti uyambe kusewera kumbuyo?

Idangokhala pulani ya Mulungu chifukwa kochi wa timuyi panthawiyo, Meke Mwase, adandifunsa za malo amene ndimasewera ndiye ndidangoti kumbuyo. Basitu kuyamba kusewera kudali komweko.

 

Zidayamba kukuyendera m’chaka chanji?

Mu 2010. Chaka chimenechi ndidasankhidwanso wosewera amene wachita bwino kumbuyo. Koma kuchoka nthawiyo mpaka 2013 ndiye zidavuta chifukwa ndidavulala msana.

 

Wafala paliponse ndi luso lako, kodi ndi mankhwala?

Mbale wanga, Mulungu akakonza palibe amene angatsutse. Pamene sizimayenda ndimalimbikirabe kuti tsiku lina zidzayende. Palibe mankhwala koma mphamvu yake basi. Si nzeru zanga koma chifundo chake cha Mulungu.

 

Malo amene ukusewera ku Flames umalimbirana ndi Francis Mlimbika, kodi simuchitirana nsanje?

Francis ndi mbale wanga, ndimamupatsa ulemu ndipo ndimakondwera naye. Dziwani kuti nayenso Mulungu adamupatsa luso. Ngati lusolo lili la Mulungu, ine ndani kuti ndimuchitire nsanje?

 

Kodi ukungotchula za Mulungu bwanji? Uli mpingo wanji?

Mbale wanga, palibe munthu amene sadziwa kuti kumwamba kuli Mulungu. Ngakhale wakuba amadziwa. Tili m’masiku omaliza, palibe chomwe tingachite ngati iye palibe. Malembo amati ngati Iye samanga nyumba omangayo amanga pachabe. N’chifukwanso ndimatsogoza Mulungu pazonse. Ndikupemphera mpingo wa Seventh Day Adventist.

 

Ukutchulidwa maina osiyanasiyana, kodi mainawa adabwera bwanji?

Tili ku Cosafa, onenerera mpira amanditchula kuti Soul Brother ati chifukwa cha tsitsi langali limafanana ndi oimba a gulu la Soul Brothers kumeneko. Kunoko anthu andipatsa dzina loti Headmaster chifukwa ndimapisira malaya 90 minitsi.

 

Kodi sumeta chifukwa chiyani? Nanga kupisiraku?

Ndimasangalala ndi osewera mpira akale amene samameta wamba, mametedwe alerowa kudalibe. Komanso amapisira ngakhale ma jersey ndi makabudula awo adali aang’ono. Zimenezi zimandisangalatsa. Komanso ndimamukumbukira Chisomo Kamulanje amene adandiuza zambiri za malo amene ndimasewera aja. Pamene amachoka ku Bullets ndidanena kuti ndikufuna ndidzapange chinthu chomwe ndidzamukumbukire nacho.

Tags: Yamikani Fodya
Previous Post

Anatchezera

Next Post

Catholics commemorate Communications Day

Related Posts

Patrick sakubwerera mmbuyo pa chikopa
Nkhani

Patrick Mwaungulu ndi katakwe pokankha chikopa

July 24, 2022
Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Next Post
To be invited: Pope Francis

Catholics commemorate Communications Day

Opinions and Columns

My Turn

Bitcoin and regulations

August 8, 2022
Editor's Note

My beautiful experience as an intern

August 7, 2022
Editor's Note

My beautiful experience as an intern

August 7, 2022
Big Man Wamkulu

What is he up to? He doesn’t drink

August 7, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Chizuma: She had medical consultations

    ACB clarifies Buluma’s absence for trial

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Court rebuffs MultiChoice Malawi on new tariffs

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Rip-off 

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Treasury Secretary says won’t resign

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Judiciary under probe 

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.