Tuesday, September 26, 2023
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Chilimikani pa ulimi—Kazembe

by Martha Sande
09/02/2018
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Malinga ndi ng’amba imene yasautsa m’madera ambiri m’dziko lino, wachiwiri kwa kazembe wa limodzi mwa maiko a ku Ulaya la Flanders, Nikolas Bosscher wati boma la Malawi liyenera kuika mtima potukula ulimi m’dziko muno.

Bosscher adanena izi Lolemba pa msonkhano wa dzidzidzi wa komiti ya National Agricultural Content Development Committee (NACDC).

Iye adati kuti dziko lino lithane ndi mavuto akudza chifukwa cha kusintha kwanyengo, n’kofunika kubweretsa chitukuko chachikulu kumbali ya ulimi.

“Dziko la Malawi silikuchita chitukuko chenicheni kumbali ya ulimi chifukwa ndalama zambiri zikumapita kundondomeko yopereka zipangizo zaulimi motsika mtengo ndi kugula chimanga zomwe sizingamange maziko olimba otukula ulimi,” adatero iye.

Iye adati ulimi ukumakhudzidwa ndi china chilichonse chokudza monga ng’amba, tizilombo toononga mbewu, matenda ngakhale kusowa kwa misika kumene. Choncho boma liyenera kuika patsogolo ndikubweretsa chitukuko kumbali ya ulimi.

“Monga madera omwe chimanga chaumiratu, mlimi ayenera kuuzidwa kuti azule chimangacho ndikubzala mbewu zina monga chinangwa ndi mbatata,” adalongosola Bosscher.

Mkulu wa nthambi ya ulangizi ku unduna wa zaulimi Jerome Nkhoma yemwe adali nawo pa msonkhanowo adati boma laika kale mtima pa chitukuko ndipo mwazina lidaika mlozo womwe kampani zingatsate pobweretsa chitukuko kumbali ya ulimi.

Nkhoma adati nkofunika kuti alimi apatsidwe uthenga oyenera mwachangu okhudzana ndi ulimi pothana ndi vutoli.

Ndipo Farm Radio Trust, bungwe lomwe limathandiza kufalitsa uthenga kwa alimi, yomwe idaitanitsa msonkhanowo idati zinthu sizili bwino m’dziko muno ndipo alimi ambiri akhudzidwa ndi ng’amba ndi mbozi zomwe zikuononga mmera.

“Ngakhale tidauzidwa kuti kukhala ng’amba komanso mbozi zoononga mmera, sitimayembekezera kuti vutoli likhala lalikulu chonchi,” adatero George Vilili wochokera ku bungwelo.

Pomwe mkulu wa nthambi yoona zanyengo Jolamu Nkhokwe adati nthambi yake idanena kuti chaka chino kukhala ng’amba komanso madzi osefukira mwezi wa September chaka chatha.

Nkhokwe adati mvula ikadali kugwa, ndipo Madera ena omwe mudagwa ng’amba, alandira mvulayi komabe adalimbikitsa alimi kutsatira uthenga omwe nthambi yake imapereka nthawi ndi nthawi.

Previous Post

MEC ikufunakusinthatsiku la chisankho

Next Post

CFTA to unleash Africa’s full potential, says ECA chief

Related Posts

Nkhani

 Liwu la mafumu pa zochotsa anthu 1 miliyoni mu AIP

September 23, 2023
Nkhani

Boma likugwiritsa K3 biliyoni pothandiza ochotsa mimba

September 23, 2023
Gogo Chabwera
Nkhani

Gogo athawa m’mudzi mwake

September 17, 2023
Next Post

CFTA to unleash Africa’s full potential, says ECA chief

Opinions and Columns

My Turn

Resolve DStv spat amicably

September 25, 2023
People’s Tribunal

Time for politicians to memorise the myth of Sisyphus

September 24, 2023
Big Man Wamkulu

I hear he is engaged to somebody

September 24, 2023
Musings on Corruption

Is ‘God-fearing’just a façade?

September 24, 2023

Trending Stories

  • Kept report under wraps: Chakwera

    Inside ‘hidden’ Reforms report

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Mysterious animal injures 9 people

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • RBM wants suspension of judgement in ICT deal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Strange illness scare forces school to close

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Court summons MDF on Chilima evidence

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2023 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.