Nkhani

Mugwiliranji bere la mwini?

Listen to this article

Masiku apitawa mtsikana wina  adandifotokozera za momwe mphongo ina idagwirira bere lake pa msewu mumzinda wa  Lilongwe.

Mtsikanayu adali akungodziyendera  mutauniyo pomwe adangodzidzimuka mkono wa bambo yemwe amabwera kutsogolo kwake  uli pabere lake.

Mmene amati azilankhula, bamboyo nkuti  atayamba kuyenda kupitiriza ulendo wake ngati sadachite kalikonse.

Mtsikanayo adangoti kakasi, kenaka  adangopitiriza ulendo wake ali cheucheu kuti bambo wina  asamuonererenso.

Nkhaniyi idandikumbutsa zomwe  zidandionekera mutauni ya Limbe, ku Blantyre, zaka zinayi kapena zisanu  zapitazo.

Anthu adali pilingupilingu m’mawa wa  Loweruka limenelo ndipo ndidali pandawala kukwakwera basi pomwe  ndidangozindikira mkono wa mnyamata wina, yemwe ndidali ndisadamuoneko  chibadwire, uli pabere langa.

Ndikudzidzimuka, mnyamatayo, yemwe  timayenda mosemphana, adapitirira ulendo wake akumwetulira ngati sadachite  chilichonse chodabwitsa.

Ndidangoti kakasi, kusowa cholankhula  mnyamatayo akulowelera m’gulu la anthu omwe anali akuyenda pamalopo.

Amayi ndi atsikana omwe zangati izi  zidawaonekerapo angachitire umboni za mkwiyo ndi manyazi omwe amadza zoterezi  zikakuchitikira, poti ena zawachitikira m’maofesi, kusukulu ndi malo  ena.

Kwa nthawi yaitali ndidakhala  ndikudzifunsa za mmene ndikadakhaulitsira ndoda yachipongweyo.

Ndikadakuwa? Koma ndi changu chimene  mnyamatayu adachita, ndimakaika ngati ena omwe amadutsa pamalopo adaona zomwe  zidachitika. Akadandikhulipilira ndani? Umboni sukadavuta kodi?

Kapena ndikadamumenya? Koma  mwachidziwikire akadabwenzera ndipo mwinanso nkadavulazidwa ndine  ndemwe.

Ena nkumati atsikana mukumadziitanira  mavuto nokha kaamba kamavalidwe kosadzilemekeza, koma ichi sichifukwa chokwanira  mpang’ono pomwe choti anthu ena azichita zomwe afuna ndi matupi a  amayi.

Kaya wina atavala zoonetsa mawere ake,  palibe choyenereza bambo kapena mnyamata kugwira mawerewo. Tisaiwale kuti  m’dziko muno muli ufulu wa kavalidwe.

Kwa amayi, ndikukhulupilira kuti  kungopenya ngati momwe ndidachitira ine ndi msungwana wa ku Lilongweyu,  sikungathandize kwenikweni.

Ngati pali chomwe mungathe kuchita kuti  abambo oterewa aonekere poyera, chitani, kuti aone polekera.

Related Articles

Back to top button