Tuesday, August 9, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Abusa awaganizira kupereka pathupi

by Martha Chirambo
13/03/2022
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Ali ndi zaka 17, mwanayu ankadwala matenda a muubongo omwe adabweretsanso mavuto olankhula pamoyo wake.

Koma chimodzi chomwe mwanayu amakonda ndi kusonkhana nawo m’malo a mapemphero. Uku ndi komwe mwanayu akuti amapeza chilimbikitso pamoyo wake.

Komatu n’zachisoni kuti kumalo komwe mwanayu amapezako chilimbikitso walandirako mavuto. Wapezeka ndi pathupi pa miyezi inayi ndipo watchula abusa a mpingo wina m’boma la Mzimba kuti ndiwo eni pathupipo.

Msangulutso udafika pakhomo pa mwanayo yemwe amakhala ndi agogo ake ku Mzimbako.

Agogowo adati mwanayo amapemphera kumpingoko ndipo atazindikiridwa kuti ali ndi mimba, adatchula abusawo.

“Nkhaniyo idatikulira ndipo tidakaitula kupolisi komwe adatiyankha kuti popeza mwanayu ali ndi zaka 17, sangatsegule mlandu wogwirira mwana koma tikangosuma kukhoti kuti abusawo azimuthandiza,” anatero abambowo.

Iwo adati adakadula chisamani ndipo nkhaniyi iyamba kulowa m’khoti pa 14 March.

Agogowo adatinso mwanayo amadwala matenda a muubongo kuchokera ali wachichepere omwe amauchititsa kuti nthawi zina azilepheranso kulankhula.

Koma makolowo adati sakukhutitsidwa ndi zomwe adauzidwa kupolisi chifukwa m’dzukulu wawo akadali wamng’ono komanso amadwala matenda a muubongo choncho akufuna abusawo akanazengedwa mlandu ngakhale abusawo anavomera pamaso pa apolisi kuti mimba ndi yawo.

“Ati satana anawanyenga,” adatero abambowo.

Chodabwitsa n’choti abusawo ali ndi udindo waukulu pakati pa abusa a mipingo yonse ku Mzimba ndipo amatenganso gawo lalikulu lophunzitsa zopewa ndi kuteteza ana, achinyamata komanso amayi kunkhanza.

Polankhulapo wogwira ntchito yoteteza ana m’deralo a Washington Phiri anati n’zokhumudwitsa kuti mwanayu wagwiriridwa kachiwiri ndi abambo awiri osiyana.

A Phiri adati n’zodabwitsanso kuti chaka chatha atagwiriridwa makolo a mwanayo adalembetsa kuti ali ndi zaka 15 zomwe zikutanthauza kuti chaka chino amafunika akhale ndi zaka 16.

“Chaka chatha, mwanayu adagwiriridwaponso ndi bambo wina yemwe anathawa nkhaniyi titakaitura ku polisi,” adatero Phiri.

Katswiri pa nkhani zokhudza maufulu a ana komanso amaimira anthu pa milandu yokhudza nkhani za maufulu a Wesley Mwafulirwa adati abusawa akhoza kuzengedwa mlandu wogwiririra munthu wodwala matenda a muubongo.

“Mlandu wochita za dama ndi munthu yemwe pali umboni wokwanira kuti amadwala matenda a muubongo suyendera zaka. Ngakhale zaka zitakhala zambiri, umakhalabe mlandu waukulu malinga ndi malamulo a dziko lino,” adatero a Mwafulirwa.

Nawo akulu apolisi ku Euthini a Rhodes Chitera adati pa nkhani ya zaka za mwanayu makolo ake anenetsa kuti ali ndi zaka 17, zomwe zachititsa kuti apolisi asatsegule mlandu wogwiririra mwana.

“Tidayesetsa kuti tilowerenso kumbali ya matenda a muubongo, koma makolowa anakanitsitsa kuti mwana wawoyo akudwala. Makolowo anangotiuza kuti mwanayo anadwala kwambiri ali wachichepere,” anatero a Chitera.

Apa iwo adatkizanso kuti apolisi akukonza njira zoti mwanayu apite kuchipatala chachikulu mumzinda wa Mzuzu akamuyeze kuti apolisi akhale ndi umboni wogwirika wa matenda ake akamatsegula mlandu.

Previous Post

The dilemma of handling relationships as a single parent

Next Post

Kalibu cherishes student for AC Milan Academy trials

Related Posts

Patrick sakubwerera mmbuyo pa chikopa
Nkhani

Patrick Mwaungulu ndi katakwe pokankha chikopa

July 24, 2022
Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Next Post

Kalibu cherishes student for AC Milan Academy trials

Opinions and Columns

My Turn

Bitcoin and regulations

August 8, 2022
Editor's Note

My beautiful experience as an intern

August 7, 2022
Editor's Note

My beautiful experience as an intern

August 7, 2022
Big Man Wamkulu

What is he up to? He doesn’t drink

August 7, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Macra ordered MultiChoice Malawi not to 
implement the new proposed tariffs

    Court rebuffs MultiChoice Malawi on new tariffs

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Treasury Secretary says won’t resign

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Judiciary under probe 

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chakwera’s austerity measures questioned

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Nankhumwa rally irks DPP governor

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.