Nkhani

Adzudzula MEC

Katswiri wa ndale wa sukulu yaukachenjede ya University of Livingstonia (Unilia), George Phiri, wati bungwe la MEC lidalakwa kuimitsa chisankho cha mphungu wa Nyumba ya Malamulo wa kummwera kwa boma la Lilongwe.

Chisankhochi chimayembekezereka kuchitika Lachiwiri pa November 5, koma bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) lidachiimitsa kaamba ka ziwawa zomwe zimachitika m’derali.

Kuponya voti ndi ufulu wa munthu wina aliyense wosachepera zaka 18

Poimitsa zisankhozo mkulu wa MEC, Sam Alfandika, adati bungwe lake lidalandira malipoti wodandaula kuchokera ku chipani cholamula cha Democratic Progressive Party (DPP), komanso akuluakulu ake omwe amagendedwa akapita kukaona momwe ntchito yokonzekera chisankho imayendera.

Anthu ndi chipani cha UTM akhala akuuza MEC kuti siingachititse chisankho choti anthu n’kuchikhulupirira kaamba ka momwe idayendetsera zisankho zapatatu za pa May 21.

UTM idanyanyala kuti siichita nawo chisankhocho kaamba koti idataya chikhulupiriro mwa bungweli.

Izi zidachititsa omwe amaimira chipanichi pa chisankho cha phungu wa m’deralo kuima payekha.

Ngakhale zinthu zili choncho, anthu akudzudzula MEC kuti idalakwa kuimitsa chisankhocho kaamba koti sizikugwirizana n’zofuna za anthu.

Phiri adati boma ndi MEC achita zofuna zawo osati za anthu a m’deralo kaamba koti tsopano miyezi 7 yadutsa opanda mphungu.

“Anthu a m’derali ndiwo akuvutika kaamba koti alibe phungu wowaimira m’Nyumba ya Malamulo,” adatero.

Katswiriyu adati anthu ambiri adataya chikhulupiriro mwa MEC ndipo akuopa chibwereza cha mavuto omwe adakumana nawo pa May 21.

Phiri adati MEC siidaganizire nthawi ndi ndalama zomwe anthu alowetsa pochita misonkhano yokopa anthu ndipo sakudabwa kuti anthu ena akufuna kusumira MEC.

“Izi zikungoonetsa poyera kuti MEC siidalandire uphungu wabwino,” iye adatero.

Peter Dimba, yemwe akuimira chipani cha Malawi Congress Party (MCP), waopseza kuti akokera MEC ku khoti kaamba koti yamuongetsa ndalama.

Mkuluyu adati sakuonapo chilungamo pa ganizo la MEC losintha tsiku la chisankho anthu atalowetsa ndalama za kampeni kawiri.

Dimba adati waononga ndalama zambiri pa kampeni yokonzekera chisankho cha pa May 20, komanso cha pa November 6.

Iye adati chopweteka n’choti anthu a m’derali akhala opanda phungu kwa miyezi 7 tsopano.

“Izi zikutanthauza kuti sangapindule ndi ndalama za chitukuko za thumba la Constituency Development Fund,” adatero Dimba.

Naye Frank Mazizi yemwe akuimira DPP adadandaula kuti chisankhochi chawaika pa dzuwa.

Iye adati waononga ndalama zoposa K30 miliyoni pa kampeni ya chisankhochi.

Mazizi adati ngakhale chisankho chaimitsidwa akuonongabe ndalama poopa anthu kumuiwala.

“Sindidalandire thandizo la ndalama kuchokera ku chipani change. Izi zikutanthauza kuti zonse zikuchokera m’nthumba langa,” iye adatero.

Mazizi adagwirizana ndi Dimba kuti chitukuko m’derali sichikupita patsogolo kaamba kosowa phungu.

Related Articles

Back to top button