Saturday, August 13, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Akumba manda m’khonde la nyumba

by Wisdom Chirombo
04/10/2020
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Athu okwiya aika maliro pakhomo pa mkulu wina ku Chirimba mumzinda wa Blantyre yemwe amamanga nyumba panjira yolunjika kuchipata cha manda.

Malingana ndi ena mwa omwe adaona izi zikuchitika ati si koyamba kuti mkuluyo achite zotere chifukwa mmbuyomu adachitanso zotere.

Dalili kulongosola mbali imene malo ake achita malire ndi manda

“Poyamba adamanga mpanda wotchinga msewu wa kumanda ndipo zinatengera amfumu kulamula kuti agumule mpandawo ncholinga choti anthu azitha kudutsa mosavuta,” adatero mmodzi mwa anthuwo, yemwe adakana kutchulidwa dzina.

Kumbali yake, mkuluyo, Henderson Dalili, adati adadabwa kuona T/A Machinjiri akubwera ndi gulu la anthu omwe amati ndi okhumudwa ndi ganizo lake lomanga nyumba pamalo akepo.

“Malowa ndi anga ndipo ndimamanga nyumbayi podziwa kuti ndi malo anga. Apa ndidaona a Machinjiri akubwera ndi gulu la anthu omwe amandiopseza,” adatero Dalili.

Iye adatinso adaganiza zomanga nyumba pamalopa pozindikila kuti mandawo anali pafupi kudzadza.

“Panopa ndikufuna kukumana ndi a Machinjiri kuti ndiwauze kuti ndasiya kumanga nyumbayi ndipo ndikakambirane nawo za tsogolo la malowa,” adatero iye.

Kumbali yake T/A Machinjiri adati zoti Dalili akumanga nyumba pamanda akuzidziwa ndipo kuti anakambirana nawo kunatsala ndi kuwapatsa chigamulo cha papepala sakusamala pomanga nyumba chifukwa chikhalidwe chathu sichilola anthu a moyo kuyandikana ndi manda,” adatero Machinjiri.

Mfumu ya ndodoyo idakana kuthilapo ndemanga pankhani yokhudzana ndi kuikidwa kwa munthu wakufa pamalo pomwe Dalili akubzala maziko a nyumba.

Ndipo Gulupu Magasa ya m’deralo idati zoti a Machinjiri ndi iwo anapita kukakambilana ndi a Dalili pa zomwe achitazo ndi zoona koma adati sakudziwa zoti anthu ayika maliro pamalo omwe akuyika maziko a nyumba..

Previous Post

Aphungu akana makondomu aulere

Next Post

One-stop border key to trade facilitation—govt

Related Posts

Patrick sakubwerera mmbuyo pa chikopa
Nkhani

Patrick Mwaungulu ndi katakwe pokankha chikopa

July 24, 2022
Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Next Post

One-stop border key to trade facilitation—govt

Opinions and Columns

Bottom Up

Mindset change should target Indian-Malawians

August 12, 2022
My Turn

Legalise cannabis for poor farmers

August 12, 2022
Editor's Note

Govt set to develop Whistleblower Protection Act

August 11, 2022
Business Unpacked

How government is killing parastatals softly

August 11, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Chakwera withheld delegated duties from Chilima

    Did ACB, LMC rush? 

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Minister allays Shoprite exit fears

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Mindset change should target Indian-Malawians

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Covid-19 pushes Kuhes into drug manufacturing

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • No DPP candidate endorsements from us—APM

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.