Sunday, August 14, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Ana akagonana azimangidwa?

by Martha Chirambo
10/07/2021
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Bwalo lalikulu la milandu Lachitatu likudzali likhala likumva mlandu umene mnyamata wina wa zaka 15 (sitimutchula dzina) wasumira boma.

Mnyamatayo adakamang’ala kubwalolo apolisi adamugwira ndi kumuzenga mlandu woti adagona ndi mwana.

Chijozi: Anyamata okha ndiwo amamangidwa

Gawo 138 (1) la mnalamulo a dziko muno limati ndi mlandu kugona ndi mwana wa zaka zosaposa 16 koma mnyamatayo akufuna kumvetsetsa ngati apolisi ali ndi mphamvu yomanga mnyamata yekha ana atagwirizana zokhalira malo amodzi.

Woimira mwanayo ndi a Chikondi Chijozi komanso a Ruth Kaima mmalo mwa bungwe lounika za malamulo kummwera kwa Africa la Southern African Litigation Centre (SALC). Iwo akufuna bwalolo liunikire ngati mlandu wa mwanayo ungapitirire kubwalo la majisitiliti.

A Chijozi adati cholinga chawo n’kuteteza ana aamuna.

“Ana okulirapo amapanga zibwenzi ngati ana okhaokha, koma masiku ano anawa akagwidwa, mwana wa mwamuna yekha ndiye akumamangidwa. Ife tikufuna khoti liunike bwino pamenepa,” adatero a Chijozi.

Iwo adati akufuna kuti papezeke njira zina zolangizira anawa osati kukalowa kundende.

“Mlandu uzikhalapo ngati mwana wokulirapo mwina wa zaka 15, wagwiririra mwana wochepa msinkhu koma osati kuzenga milandu ana oti adali pa ubwenzi wogonana,” iye adalongosola.

Mlanduwu walowa khoti pomwenso pa June 21, mwezi watha, bwalo la milandu la majisitiliti mumzinda wa Blantyre lidagamula kuti mnyamata wina wa zaka 18 yemwe adali pa ubwenzi wogonana ndi mtsikana wina wa zaka 15 alibe mlandu wogwiririra.

M’chigamulocho, woweruza milandu a Elijah Blackboard Dazilikwiza Daniels adauza a boma kuti amutulutse kundende mnyamatayu komwe adakhalako kwa miyezi 8, chim’mangireni chaka chatha chifukwa adalibe mlandu uliwonse.

Mmodzi mwa omenyera ufulu wa ana, a Desmond Mhango adauza wailesi ya Capital FM mkati mwa sabatayi kuti  anawa asamatumizidwe kundende pa nkhanizi.

Iwo adati lamulo logwiririra ana limati munthu wamkulu amangidwe akamagona mwana wamg’ono.

“Ndi zodabwitsa kuti anawa akumazengedwa milandu m’makhoti akuluakulu osatinso makhoti a ana,” adatero a Mhango.

Previous Post

Must Charity golf raises K103m

Next Post

Trapped in unwanted pregnancies

Related Posts

Patrick sakubwerera mmbuyo pa chikopa
Nkhani

Patrick Mwaungulu ndi katakwe pokankha chikopa

July 24, 2022
Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Next Post
About 20 percent of women with 
Covid-19 in hospitals died

Trapped in unwanted pregnancies

Opinions and Columns

People’s Tribunal

Time is not on the side of PDP

August 14, 2022
Big Man Wamkulu

She is very elusive, loves money

August 14, 2022
My Thought

Stop cyber harassment

August 14, 2022
Off the Shelf

Government, through Mera, killing Escom

August 13, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • World Bank suggests kwacha re-alignment

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  •   MPs on trial

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Wanderers pen Sulom over refs

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Did ACB, LMC rush? 

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Electricity tariff proposal to face scrutiny—mera  

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.