Nkhani
Kudziongola ngati zenizeni, koma ayi
Lachitatu sabata yatha anyamata a Flames, ngakhale adapeza mwayi wochuluka kuposa Namibia, adalepherana ndi timuyo mumpikisano wolimbirana malo ku mpikisano wa chikho cha dziko lonse.
Zodabwitsa zidalipo zingapo. Poyamba, ambiri mwa anyamata amene adayesana ndi timu ya Zimbabwe pokonzekera masewerowa sadamenye. Chachiwiri n’chakuti mmalo moona kuti anyamata adamenyawo akadachita zakupsa kutsogolo mmalo mwa omwe adamenyawo, mphunzitsi wa timuyo palibe chomwe adachita. Apa anyamatawo akudziongola pokonzekera mpirawo. Kukhala ngati amwetsa zigoli koma ayi.